< Yohane 12 >
1 Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa.
За шість днів до Пасхи Ісус прийшов до Віфанії, де був Лазар, якого воскресив із мертвих.
2 Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho.
Там Йому приготували вечерю. Марта слугувала, а Лазар був одним із тих, хто сидів із Ним за столом.
3 Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.
Тоді Марія взяла літру з дуже дорогим чистим нардовим миром, намастила ноги Ісуса й своїм волоссям обтерла Його ноги. І дім наповнився пахощами мира.
4 Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati,
Але Юда Іскаріот, один з Його учнів, який мав Його зрадити, сказав:
5 “Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi.
―Чому б не продати це миро за триста динаріїв та не роздати бідним?
6 Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.
Він казав так не тому, що піклувався про бідних, а тому, що був злодієм. Йому було доручено носити скриню з грошима, але він брав із неї гроші.
7 Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga.
Ісус сказав: ―Залиши її, вона зберігала це на день Мого похорону.
8 Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”
Бідних ви завжди маєте з собою, а Мене не завжди матимете.
9 Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa.
Тим часом багато юдеїв дізналося, що Він там. Вони прийшли не тільки заради Ісуса, але й подивитись на Лазаря, якого Він воскресив із мертвих.
10 Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro,
Тоді первосвященники змовилися вбити й Лазаря.
11 pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.
Адже багато юдеїв залишало їх і вірило в Ісуса.
12 Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu.
Наступного дня багато людей, які прийшли на свято, почувши, що Ісус іде в Єрусалим,
13 Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti, “Hosana! “Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye! “Yodala Mfumu ya Israeli!”
взяли пальмові гілки, вийшли Йому назустріч та викрикували: «Осанна!» «Благословенний Той, Хто йде в ім’я Господа!» «Цар Ізраїля!»
14 Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:
Ісус, знайшовши осля, сів на нього, як написано:
15 “Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni; taona mfumu yako ikubwera, itakhala pa mwana wabulu.”
«Не бійся, дочко Сіону: Ось Цар твій їде верхи на молодому ослі».
16 Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.
Спочатку Його учні не розуміли цього. Але після того, як Ісус був прославлений, вони згадали, що це було написано про Нього й що це збулося з Ним.
17 Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni.
Люди, які були з Ісусом, коли Він покликав Лазаря з гробу й воскресив його з мертвих, свідчили [про це].
18 Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi.
Тому багато людей вийшли Йому назустріч, бо чули, що Він здійснив це знамення.
19 Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”
Тоді фарисеї почали казати один одному: «Бачите, що нічого не допомагає? Ось [увесь] світ пішов за Ним!»
20 Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando.
Серед тих, хто прийшов поклонитися на свято, було декілька греків.
21 Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.”
Вони підійшли до Филипа, який був із Віфсаїди, що в Галілеї, і просили його: «Пане, ми хочемо побачити Ісуса».
22 Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.
Филип пішов і сказав Андрієві, і тоді Андрій та Филип розповіли про це Ісусові.
23 Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe.
Ісус відповів їм: ―Прийшов час прославитись Синові Людському.
24 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’
Істинно кажу вам: якщо зерно пшениці, впавши в землю, не вмирає, то залишається одне. Але якщо вмирає, дає великий врожай.
25 Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios )
Кожен, хто любить своє життя, втратить його, а хто ненавидить своє життя в цьому світі, збереже його для вічного життя. (aiōnios )
26 Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.
Хто служить Мені, той повинен слідувати за Мною; і де Я є, там буде і Мій слуга. Якщо хтось буде служити Мені, Мій Отець шануватиме його.
27 “Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi.
Тепер Моя душа стривожена, і що Мені сказати? Отче, врятуй Мене від цієї години? Але саме заради цієї години Я і прийшов.
28 Atate, lemekezani dzina lanu!” Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.”
Отче, прослав Своє ім’я! Тоді почувся голос із неба: «Я прославив і знову прославлю!»
29 Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”
Натовп, який був там, почувши це, сказав, що прогримів грім, а інші казали, що ангел говорив із Ним.
30 Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine.
Ісус відповів: ―Не для Мене пролунав цей голос, а для вас.
31 Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa.
Зараз настав суд для цього світу. Тепер правителя цього світу буде вигнано геть.
32 Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.”
Але коли Я буду піднятий від землі, Я всіх притягну до Себе.
33 Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.
Він сказав це, щоб показати, якою смертю має померти.
34 Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn )
Тоді люди сказали Йому: ―Ми чули із Закону, що Христос житиме вічно. Як же Ти кажеш, що «Син Людський має бути піднятий?» Хто Цей Син Людський? (aiōn )
35 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita.
Тоді Ісус сказав їм: ―Світло ще трохи часу буде з вами. Ходіть, доки маєте світло, щоб темрява не охопила вас. Хто ходить у темряві, той не знає, куди йде.
36 Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.
Повірте у світло, поки у вас є світло, щоб ви стали синами світла. Ісус закінчив говорити і, відійшовши, скрився від них.
37 Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe.
Незважаючи на те, що Він зробив перед ними стільки знамень, вони не вірили в Нього.
38 Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti: “Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani, ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”
Так здійснилося слово пророка Ісаї, який сказав: «Господи, хто повірив почутому від нас і кому відкрилася рука Господня?»
39 Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:
Не могли повірити ще й тому, що, як сказав Ісая:
40 “Iye wachititsa khungu maso awo ndi kuwumitsa mitima yawo, kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo, kapena kuzindikira ndi mitima yawo, kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”
«Він зробив сліпими їхні очі і закам’янілими їхні серця, щоб вони не бачили очима, і не розуміли серцем, і не навернулися, щоб Я зцілив їх».
41 Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.
Ісая сказав це, адже побачив Його славу й говорив про Нього.
42 Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge;
Навіть серед керівників багато хто повірив у Ісуса. Але через фарисеїв вони не визнавали своєї віри, щоб їх не вигнали із синагоги.
43 pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.
Адже вони любили людську славу більше за Божу славу.
44 Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine.
Ісус голосно промовив: ―Хто вірить у Мене, той вірить не тільки в Мене, але й у Того, Хто послав Мене.
45 Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine.
Той, хто бачить Мене, бачить і Того, Хто послав Мене.
46 Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.
Я – світло, яке прийшло у світ, щоб кожний, хто вірить у Мене, не залишався в темряві.
47 “Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa.
Якщо хтось чує Мої слова, але не дотримується їх, Я не суджу його. Адже Я прийшов не судити світ, а спасти його.
48 Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa.
Для того, хто відкидає Мене й не приймає Моїх слів, є суддя. Слово, яке Я сказав, судитиме його останнього дня.
49 Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere.
Бо не від Себе Я говорив, але Отець, Який послав Мене, дав Мені заповідь, що сказати і як казати.
50 Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios )
Я знаю, що Його заповідь – це вічне життя. Тому все, що кажу, Я кажу саме так, як сказав Мені Отець. (aiōnios )