< Yohane 12 >

1 Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa.
Six days before the Passover [celebration started], Jesus arrived in Bethany [village, along with us]. That was where Lazarus lived. He was the man Jesus [previously] caused to be alive again after he died.
2 Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho.
There they gave a dinner to [honor] Jesus. Martha served the meal. [Her younger brother], Lazarus, was among the people who were eating with Jesus.
3 Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.
Then Mary took [a bottle] of expensive perfume [called] nard and poured it on Jesus’ feet [to honor him]. Then she wiped his feet with her hair. The whole house was filled with the [beautiful] smell of the perfume.
4 Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati,
But one of his disciples, Judas Iscariot, (OR, Judas, the man from Kerioth [Town]) objected. He was the one who later enabled Jesus’ enemies to seize him.
5 “Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi.
He said, “(We should have sold this perfume and given [the money] to poor people!/Why did [we] not sell this perfume and give [the money for it] to the poor people?) [RHQ] We could have gotten 300 days’ wages for it!”
6 Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.
He said that, not because he cared about the poor people, but instead, because he was a thief. He was the one who kept the bag [of funds that people gave to help Jesus and us his disciples], and he often stole some of the money that was {that [people]} put into it.
7 Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga.
Then Jesus said, “Do not bother her! [She bought this perfume] in order to save it until the day when they will bury me [after I die].
8 Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”
There will always be poor people among you, [so you can help them whenever you want to]. But I will not be with you much longer, [so it is good that she showed right now how much she appreciates me].”
9 Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa.
A large crowd of Jews heard [people say] that Jesus was there [in Bethany]. So they came, not only [to see] Jesus but also to see Lazarus, the man whom he had caused to become alive again after he died.
10 Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro,
So the chief priests decided to kill Lazarus also,
11 pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.
because many of the Jews were [deserting them and] going to Jesus and believing in him because of [Jesus causing] Lazarus [to be alive again].
12 Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu.
The next day the huge crowd of people that had come [to Jerusalem] for the [Passover] celebration heard that Jesus was coming to Jerusalem.
13 Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti, “Hosana! “Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye! “Yodala Mfumu ya Israeli!”
So they [cut] branches from some palm trees and took the branches out [of the city] to [wave them when they] met him. Some of them were shouting things like, “Hooray!” “May the Lord [God] bless the one who is coming with his authority [MTY]!” Some other people were shouting, “[May God bless] the King of Israel!”
14 Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:
When Jesus [came near to Jerusalem], he got a young donkey and sat on it [as he rode into the city]. By doing this, [he fulfilled] what had been written {what [a prophet] had written} [in Scripture],
15 “Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni; taona mfumu yako ikubwera, itakhala pa mwana wabulu.”
You people of Jerusalem, do not be afraid! Look! Your king is coming! He is riding on a donkey’s colt!
16 Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.
At first [we] disciples did not understand those things. But after Jesus had returned to heaven, we realized that those things had been written {that [a prophet] had written those things} about him, and that [by] doing those things for him [the people had fulfilled what the prophet prophesied].
17 Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni.
The crowd that was with him continued to tell other people that he called Lazarus to come out of the tomb, [and that Lazarus had then become alive again].
18 Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi.
Because of that, many people, because they heard [others say] that he had performed this miracle, went to meet him.
19 Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”
So the Pharisees said to each other, “It is obvious that we are making no progress [in trying to stop him! It looks like] [HYP] everyone [MTY] is becoming his disciple!”
20 Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando.
Among those who went up [to Jerusalem] to worship [God] during the [Passover] celebration were some Greeks.
21 Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.”
They came to Philip, who was from Bethsaida [town] in Galilee [province]. They [wanted him] to do something for them. They said, “Sir, we would like to talk with Jesus.”
22 Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.
So after Philip went and told that to Andrew, they both went and told Jesus.
23 Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe.
Then, [to show them that he must die in order to give eternal life to non-Jews like those Greeks], Jesus replied to them, “It is time for [God] to honor me, the one who came from heaven. [That will happen when I die].
24 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’
Listen to this carefully: [My life is like a seed] [MET]. If [someone] does not plant a kernel of grain in the ground, it does not change. It remains only one [seed]. But if it changes [after it is planted in the ground, it will grow and] produce many seeds.
25 Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios g166)
Anyone who strongly wants to keep on living [here on earth] will surely lose his life forever. But anyone who is willing to die [HYP] [for my sake] will surely gain eternal life. (aiōnios g166)
26 Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.
If [any of these Greeks or] anyone [else] wants to serve me, they must become my disciples. Then, [after they die], they will be where I am, [in heaven]. My Father will honor all those who serve me.
27 “Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi.
Now I am deeply disturbed. (I do not know what to say./What shall I say?) [RHQ] Should I say, ‘[My] Father, save me from this time [when I will suffer and die!’]? No, [I should not say that, because] the reason I came ([into this world/from heaven]) was that I would [suffer] [MTY] now.
28 Atate, lemekezani dzina lanu!” Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.”
My Father, show how great you are!” John 12:28b-36a Then [God] spoke [EUP] from heaven, saying, “I have already shown how great [I am], and I will do it again!”
29 Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”
The crowd that was there heard [it but they did not understand the words. Some said] it was thunder. Others said an angel had spoken to him.
30 Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine.
Jesus replied to them, “The voice that you heard speaking [was God’s voice, but] it was not for my benefit. It was for your benefit!
31 Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa.
Now is the time for [God] to judge [the people in] [MTY] the world. Now is the time when [I] will destroy [the power of Satan], the one who rules this world.
32 Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.”
But as for me, when I am lifted {when [men] lift me} up from the ground [on a cross, I will make a way for] gathering everyone to myself.”
33 Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.
He said this to show us the way in which he was going to die.
34 Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn g165)
[Someone in] the crowd answered him, “We understand from the Scriptures that the Messiah will live forever. So why do you say that the one who came from heaven, [who is the Messiah], will be lifted up {that [men] will lift up the one who came from heaven, [who is the Messiah], } on a cross? What kind of man who came from heaven are you [talking about]? (OR, That’s not the [kind] of Messiah [we are expecting]!)” (aiōn g165)
35 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita.
Then Jesus said to them, “[My message is like] [MET] a light for you. [I] will be with you for only a little while longer. Live and act [as you should] while I am still with you, [because suddenly you will have no more opportunity to hear my message! You do not want to be like] [MET] [someone] who cannot see where he is going any more [when it suddenly] becomes dark!
36 Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.
Believe in my message [MET] while you still have an opportunity to do it, in order that you may become people who have accepted my truth [MET]!” John 12:36b-43 After Jesus said those things, he left them and hid from them.
37 Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe.
Although he had done many miracles while people were watching, [most of] them refused to believe that he [is] ([the Messiah/from God]).
38 Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti: “Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani, ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”
[Their stubbornness and refusal to believe was similar to the stubbornness of the people that] the prophet Isaiah wrote about long ago: Lord, (hardly anyone has believed our message!/who has believed our message?) [RHQ] Most people refused to accept it, even though you showed them your power!
39 Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:
That was the reason why they were unable to believe. [It was like] Isaiah wrote somewhere else that God said:
40 “Iye wachititsa khungu maso awo ndi kuwumitsa mitima yawo, kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo, kapena kuzindikira ndi mitima yawo, kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”
They have [refused to understand; they acted as though they were] blind people! They were insensible in their inner beings! As a result, they have not perceived [my truth]! They have not understood it in their inner beings! They have not turned [from their sinful lives], and because of that I cannot help them!
41 Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.
Isaiah wrote that because [it was as though] he saw [ahead of time] how great Jesus would be, and he prophesied [those things] about him.
42 Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge;
Although most of the Jewish [leaders] [SYN] did not believe that Jesus is ([the Messiah/from God]), some of them believed in him. But they would not tell anyone that they believed in him, because [they were afraid that if they said that], the Pharisees would not let them worship in the synagogues.
43 pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.
They wanted people to praise them more than they wanted God to praise them.
44 Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine.
[Another day, when] Jesus [was teaching the people, he] shouted, “Those who believe in me, they are not believing in [me alone]. Instead, [it is as though] they also believe in the one who sent me.
45 Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine.
When they see me [and what I am doing, it is as though] they are seeing the one who sent me.
46 Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.
I have come into the world [to show people God’s truth], as a light [shows people what is around them]. I have come in order that people who believe in me will not remain [ignorant of God’s truth] [MET], [as those who are] in the darkness [are ignorant of what is around them].
47 “Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa.
As for those who hear my message but do not obey [its commands], I am not [the one who] judges them. [The main reason] that I came ([into the world/from heaven]) was not to judge [the people of] [MTY] the world. Instead, I came to save them [from being punished for their sins].
48 Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa.
There is something that will judge those who reject me and do not accept my message. On the judgment day [God] will condemn them [because they rejected] the message that I have told them.
49 Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere.
I have not said things from my own [authority]. Instead, [my] Father, the one who sent me, instructed me what to say and how I should say it.
50 Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios g166)
I know that [paying attention to] what he has instructed us [leads to] eternal life. So whatever I say is exactly (OR, only) what [my] Father has told me to say.” (aiōnios g166)

< Yohane 12 >