< Yohane 12 >
1 Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa.
Jesus therefore six days before the passover came to Bethany, where Lazarus was, whom Jesus raised from the dead.
2 Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho.
So they made him a supper there: and Martha served; but Lazarus was one of them that sat at meat with him.
3 Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.
Mary therefore took a pound of ointment of spikenard, very precious, and anointed the feet of Jesus, and wiped his feet with her hair: and the house was filled with the odour of the ointment.
4 Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati,
But Judas Iscariot, one of his disciples, which should betray him, saith,
5 “Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi.
Why was not this ointment sold for three hundred pence, and given to the poor?
6 Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.
Now this he said, not because he cared for the poor; but because he was a thief, and having the bag took away what was put therein.
7 Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga.
Jesus therefore said, Suffer her to keep it against the day of my burying.
8 Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”
For the poor ye have always with you; but me ye have not always.
9 Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa.
The common people therefore of the Jews learned that he was there: and they came, not for Jesus’ sake only, but that they might see Lazarus also, whom he had raised from the dead.
10 Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro,
But the chief priests took counsel that they might put Lazarus also to death;
11 pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.
because that by reason of him many of the Jews went away, and believed on Jesus.
12 Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu.
On the morrow a great multitude that had come to the feast, when they heard that Jesus was coming to Jerusalem,
13 Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti, “Hosana! “Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye! “Yodala Mfumu ya Israeli!”
took the branches of the palm trees, and went forth to meet him, and cried out, Hosanna: Blessed [is] he that cometh in the name of the Lord, even the King of Israel.
14 Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:
And Jesus, having found a young ass, sat thereon; as it is written,
15 “Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni; taona mfumu yako ikubwera, itakhala pa mwana wabulu.”
Fear not, daughter of Zion: behold, thy King cometh, sitting on an ass’s colt.
16 Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.
These things understood not his disciples at the first: but when Jesus was glorified, then remembered they that these things were written of him, and that they had done these things unto him.
17 Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni.
The multitude therefore that was with him when he called Lazarus out of the tomb, and raised him from the dead, bare witness.
18 Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi.
For this cause also the multitude went and met him, for that they heard that he had done this sign.
19 Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”
The Pharisees therefore said among themselves, Behold how ye prevail nothing: lo, the world is gone after him.
20 Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando.
Now there were certain Greeks among those that went up to worship at the feast:
21 Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.”
these therefore came to Philip, which was of Bethsaida of Galilee, and asked him, saying, Sir, we would see Jesus.
22 Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.
Philip cometh and telleth Andrew: Andrew cometh, and Philip, and they tell Jesus.
23 Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe.
And Jesus answereth them, saying, The hour is come, that the Son of man should be glorified.
24 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’
Verily, verily, I say unto you, Except a grain of wheat fall into the earth and die, it abideth by itself alone; but if it die, it beareth much fruit.
25 Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios )
He that loveth his life loseth it; and he that hateth his life in this world shall keep it unto life eternal. (aiōnios )
26 Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.
If any man serve me, let him follow me; and where I am, there shall also my servant be: if any man serve me, him will the Father honour.
27 “Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi.
Now is my soul troubled; and what shall I say? Father, save me from this hour. But for this cause came I unto this hour.
28 Atate, lemekezani dzina lanu!” Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.”
Father, glorify thy name. There came therefore a voice out of heaven, [saying], I have both glorified it, and will glorify it again.
29 Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”
The multitude therefore, that stood by, and heard it, said that it had thundered: others said, An angel hath spoken to him.
30 Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine.
Jesus answered and said, This voice hath not come for my sake, but for your sakes.
31 Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa.
Now is the judgment of this world: now shall the prince of this world be cast out.
32 Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.”
And I, if I be lifted up from the earth, will draw all men unto myself.
33 Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.
But this he said, signifying by what manner of death he should die.
34 Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn )
The multitude therefore answered him, We have heard out of the law that the Christ abideth for ever: and how sayest thou, The Son of man must be lifted up? who is this Son of man? (aiōn )
35 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita.
Jesus therefore said unto them, Yet a little while is the light among you. Walk while ye have the light, that darkness overtake you not: and he that walketh in the darkness knoweth not whither he goeth.
36 Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.
While ye have the light, believe on the light, that ye may become sons of light. These things spake Jesus, and he departed and hid himself from them.
37 Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe.
But though he had done so many signs before them, yet they believed not on him:
38 Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti: “Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani, ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”
that the word of Isaiah the prophet might be fulfilled, which he spake, Lord, who hath believed our report? And to whom hath the arm of the Lord been revealed?
39 Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:
For this cause they could not believe, for that Isaiah said again,
40 “Iye wachititsa khungu maso awo ndi kuwumitsa mitima yawo, kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo, kapena kuzindikira ndi mitima yawo, kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”
He hath blinded their eyes, and he hardened their heart; Lest they should see with their eyes, and perceive with their heart, And should turn, And I should heal them.
41 Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.
These things said Isaiah, because he saw his glory; and he spake of him.
42 Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge;
Nevertheless even of the rulers many believed on him; but because of the Pharisees they did not confess [it], lest they should be put out of the synagogue:
43 pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.
for they loved the glory of men more than the glory of God.
44 Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine.
And Jesus cried and said, He that believeth on me, believeth not on me, but on him that sent me.
45 Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine.
And he that beholdeth me beholdeth him that sent me.
46 Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.
I am come a light into the world, that whosoever believeth on me may not abide in the darkness.
47 “Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa.
And if any man hear my sayings, and keep them not, I judge him not: for I came not to judge the world, but to save the world.
48 Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa.
He that rejecteth me, and receiveth not my sayings, hath one that judgeth him: the word that I spake, the same shall judge him in the last day.
49 Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere.
For I spake not from myself; but the Father which sent me, he hath given me a commandment, what I should say, and what I should speak.
50 Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios )
And I know that his commandment is life eternal: the things therefore which I speak, even as the Father hath said unto me, so I speak. (aiōnios )