< Yohane 11 >
1 Tsopano munthu wina dzina lake Lazaro anadwala. Iye anali wa ku Betaniya, mudzi wa Mariya ndi mchemwali wake Marita.
Pewnego dnia zachorował Łazarz, brat Marii i Marty z Betanii.
2 Mariyayo ndi yemwe uja amene anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake. Lazaro wodwalayo anali mlongo wake.
Maria była tą kobietą, która namaściła olejkiem stopy Pana i wytarła je swoimi włosami.
3 Choncho alongo ake anatumiza mawu kwa Yesu kuti, “Ambuye, uja amene Inu mumamukonda akudwala.”
Siostry wysłały do Jezusa wiadomość: „Panie, Twój bliski przyjaciel zachorował”.
4 Atamva izi, Yesu anati, “Kudwalako safa nako. Koma akudwala kuti Mulungu alemekezedwe; ndi kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe chifukwa cha matendawo.”
Gdy Jezus to usłyszał, powiedział: —Ta choroba nie zakończy się śmiercią, lecz przyniesie chwałę Bogu i Ja, Syn Człowieczy, również zostanę dzięki niej otoczony chwałą.
5 Yesu anakonda Marita, mchemwali wake ndi Lazaro.
Jezus bardzo kochał całą trójkę: Martę, jej siostrę—Marię oraz Łazarza.
6 Koma atamva kuti Lazaro akudwala, Iye anakhalabe kumene anali masiku ena awiri.
Jednak jeszcze dwa dni pozostał tam, gdzie zastała Go ta wiadomość.
7 Kenaka anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tibwerere ku Yudeya.”
Dopiero wtedy oznajmił uczniom: —Chodźmy jeszcze raz do Judei.
8 Ophunzira akewo anati, “Rabi, posachedwa pomwepa Ayuda anafuna kukugendani ndi miyala, koma Inu mukupitanso komweko?”
—Nauczycielu! Przecież tamtejsi przywódcy chcieli Cię zabić, a Ty znowu tam idziesz?—zaprotestowali.
9 Yesu anayankha kuti, “Kodi sipali maora khumi ndi awiri pa tsiku? Munthu amene amayenda masana sapunthwa, popeza akuona chifukwa cha kuwala kwa dziko lapansi.
—Czy dzień nie ma dwunastu godzin?—odpowiedział Jezus. —Kto chodzi w ciągu dnia, nie potknie się, bo jest jasno.
10 Koma amene akuyenda usiku amapunthwa, chifukwa kuwalako alibe.”
Kto zaś chodzi nocą, potyka się, bo panuje ciemność.
11 Iye atatha kunena izi, anapitirira kuwawuza iwo kuti, “Bwenzi lathu Lazaro wagona tulo; koma Ine ndikupita kumeneko kukamudzutsa.”
Nasz przyjaciel Łazarz zasnął, muszę więc pójść, aby go obudzić.
12 Ophunzira ake anayankha kuti, “Ambuye, ngati wagona adzapeza bwino.”
—Panie! Jeśli zasnął, to znaczy, że powraca do zdrowia—ucieszyli się uczniowie.
13 Yesu ankayankhula za imfa yake koma ophunzira ake ankaganiza kuti amanena za tulo chabe.
Jezus jednak miał na myśli śmierć Łazarza. Oni natomiast myśleli, że mówi o zwykłym śnie.
14 Ndipo kenaka anawawuza momveka kuti, “Lazaro wamwalira.
Wyjaśnił im więc: —Łazarz umarł.
15 Ine ndikukondwera chifukwa cha inu kuti kunalibe kumeneko; koma kuti mukakhulupirire tiyeni tipiteko.”
Ale ze względu na was cieszę się, że Mnie tam nie było. Chcę bowiem, abyście uwierzyli. Chodźmy do niego!
16 Pamenepo Tomasi, wotchedwa Didimo, anati kwa ophunzira anzake, “Tiyeni nafenso tipite, kuti tikafere naye pamodzi.”
—Chodźmy więc! Najwyżej umrzemy razem z nim—odezwał się Tomasz, zwany Bliźniakiem.
17 Yesu atafika, anapeza kuti Lazaro anali atagona mʼmanda masiku anayi.
Gdy Jezus dotarł na miejsce, Łazarz już od czterech dni spoczywał w grobie.
18 Mudzi wa Betaniya unali pafupi ndi Yerusalemu pa mtunda wosachepera makilomita atatu,
A Betania leżała blisko Jerozolimy, w odległości niecałych trzech kilometrów,
19 ndipo Ayuda ambiri anabwera kwa Marita ndi Mariya kudzawatonthoza pa imfa ya mʼbale wawo.
dlatego wielu ludzi z Jerozolimy przyszło do Marty i Marii, aby wyrazić im swoje współczucie po stracie brata.
20 Pamene Marita anamva kuti Yesu akubwera, anapita kukakumana naye. Koma Mariya anatsala ku nyumba.
Gdy Marta dowiedziała się, że nadchodzi Jezus, wybiegła Mu na spotkanie. Maria zaś została w domu.
21 Marita anati kwa Yesu, “Ambuye, mukanakhala muli kuno, mlongo wanga sakanamwalira.
Spotkawszy Jezusa, Marta powiedziała: —Panie, gdybyś tu był, mój brat by nie umarł!
22 Koma ine ndikudziwa kuti ngakhale tsopano Mulungu adzakupatsani chilichonse chimene mudzamupempha.”
Ale jestem przekonana, że nawet teraz Bóg da Ci to, o co Go poprosisz.
23 Yesu anati kwa iye, “Mlongo wako adzauka.”
—Twój brat zmartwychwstanie—powiedział Jezus.
24 Marita anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti adzauka pa kuukanso pa tsiku lomaliza.”
—Tak, wiem o tym—odrzekła Marta. —Ożyje w dniu ostatecznego zmartwychwstania.
25 Yesu anati kwa iye, “Ine ndine kuuka ndi moyo. Wokhulupirira Ine, angakhale amwalira adzakhala ndi moyo.
—To Ja jestem zmartwychwstaniem i życiem—oznajmił Jezus. —Kto wierzy Mi, choćby umarł, będzie żyć.
26 Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?” (aiōn )
A każdy, kto żyje i wierzy Mi, nigdy nie umrze. Czy wierzysz w to? (aiōn )
27 Marita anamuwuza Iye kuti, “Inde Ambuye, ine ndikukhulupirira kuti ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu, amene abwera mʼdziko lapansi.”
—Tak, Panie—odrzekła Marta—wierzę, że jesteś Synem Boga, Mesjaszem, który miał przyjść na świat.
28 Ndipo iye atanena izi anabwerera ndi kukayitana mchemwali wake Mariya namuyankhula monongʼona pambali, nati, “Aphunzitsi abwera ndipo akukuyitana.”
Po tych słowach odeszła. Zawołała siostrę, Marię, i na osobności powiedziała jej: —Nauczyciel już przyszedł i chce się z tobą zobaczyć.
29 Mariya atamva izi, anayimirira mofulumira napita kwa Iye.
Maria natychmiast wstała i pobiegła do Niego.
30 Tsopano nʼkuti Yesu asanalowe mʼmudzi, koma anali akanali pa malo pamene Marita anakumana naye.
Jezus nie wszedł jeszcze do wsi, ale czekał tam, gdzie Go spotkała Marta.
31 Ayuda amene ankamutonthoza Mariya mʼnyumba, anaona mmene iye anayimira mofulumira ndi kutuluka kunja, iwo anamutsata akuganizira kuti ankapita ku manda kukalirira kumeneko.
Przybysze z Jerozolimy, którzy byli z Marią w domu i pocieszali ją, zauważyli, że w pośpiechu wstała i wyszła. Pomyśleli więc, że idzie wypłakać się przy grobie Łazarza, dlatego poszli za nią.
32 Mariya anafika pamalo pamene panali Yesu ndipo atamuona, anagwa pa mapazi ake ndipo anati, “Ambuye mukanakhala muli kuno mlongo wanga sakanamwalira.”
Gdy Maria doszła do Jezusa i zobaczyła Go, upadła Mu do nóg i powiedziała: —Panie, gdybyś tu był, mój brat by nie umarł.
33 Yesu ataona iye akulira, ndi Ayuda amene anabwera naye akuliranso, anakhudzidwa kwambiri ndi kuvutika mu mzimu.
Jezus zobaczył, jak Maria płacze, a wraz z nią ci, którzy za nią przyszli. Wtedy głęboko się wzruszył i zasmucił.
34 Iye anafunsa kuti, “Kodi mwamuyika kuti?” Iwo anayankha kuti, “Ambuye tiyeni mukaone.”
—Gdzie go pochowaliście?—zapytał. —Panie, chodź i zobacz—odpowiedzieli.
36 Pamenepo Ayuda anati, “Taonani mmene Iye anamukondera Lazaro!”
—Musiał być mu bardzo bliski!—zauważyli przybysze z Jerozolimy.
37 Koma ena a iwo anati, “Iye amatsekula maso a munthu wosaona, kodi sakanakhoza kuletsa kuti munthu uyu asamwalire?”
—Przecież przywrócił wzrok niewidomemu! Nie mógł więc sprawić, żeby Łazarz nie umarł?—mówili z wyrzutem niektórzy.
38 Yesu atakhudzidwanso kwambiri anafika ku manda. Manda akewo anali phanga ndipo anatsekapo ndi mwala.
Poruszony do głębi, Jezus dotarł do grobowca. Była to grota, a jej wejście zamykał głaz.
39 Yesu anati, “Chotsani mwala.” Marita mlongo wa womwalirayo anati, “Koma Ambuye, nthawi ino wayamba kununkha, pakuti wakhala mʼmenemu masiku anayi.”
—Odsuńcie głaz!—polecił Jezus. —Panie, ciało już cuchnie! Leży tam już bowiem od czterech dni—zawołała Marta, siostra zmarłego.
40 Kenaka Yesu anati, “Kodi Ine sindinakuwuze kuti ngati iwe ukhulupirira, udzaona ulemerero wa Mulungu?”
—Przecież powiedziałem ci, że jeśli uwierzysz, ujrzysz Bożą chwałę—odpowiedział Jezus.
41 Choncho iwo anachotsa mwalawo. Kenaka Yesu anayangʼana kumwamba ndikuti, “Atate, Ine ndikukuthokozani chifukwa mumandimvera.
Odsunięto więc głaz. A Jezus podniósł oczy ku górze i rzekł: —Ojcze, dziękuję Ci, że Mnie wysłuchałeś.
42 Ine ndimadziwa kuti Inu mumandimvera nthawi zonse, koma Ine ndanena izi chifukwa cha anthu amene ayima pano, kuti iwo akhulupirire kuti Inu munandituma Ine.”
Ja wiem, że zawsze Mnie wysłuchujesz, ale mówię to ze względu na tych ludzi, aby uwierzyli, że to Ty Mnie posłałeś.
43 Yesu atanena izi, Iye anayitana ndi mawu ofuwula kuti, “Lazaro, tuluka!”
Potem zawołał donośnym głosem: —Łazarzu! Wyjdź!
44 Munthu womwalirayo anatuluka, womangidwa miyendo ndi manja ndi nsalu za ku manda, ndi nkhope yake yokulungidwa nsalu. Yesu anawawuza kuti, “Mʼmasuleni, ndipo muloleni apite.”
Wtedy zmarły wyszedł z grobu. Jego stopy i ręce były jeszcze powiązane płóciennymi opaskami, a twarz owinięta chustą. —Rozwiążcie go i pozwólcie mu chodzić—rzekł Jezus.
45 Choncho Ayuda ambiri amene anabwera kudzamuchereza Mariya ndi kuona zimene Yesu anachita anamukhulupirira Iye.
Wówczas wielu ludzi z Jerozolimy, którzy przyszli z Marią i zobaczyli ten cud, uwierzyło Jezusowi.
46 Koma ena a iwo anapita kwa Afarisi ndi kukawawuza zimene Yesu anachita.
Niektórzy jednak odeszli stamtąd i powiadomili o wszystkim faryzeuszy.
47 Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anayitanitsa msonkhano wa akulu olamulira. Iwo anafunsa kuti, “Kodi ife tikuchita chiyani? Pano pali munthu uyu akuchita zizindikiro zodabwitsa zambiri.
Ci zaś, razem z najwyższymi kapłanami, zwołali posiedzenie Wysokiej Rady. —Co robić?—zastanawiali się. —Ten człowiek dokonuje tak wielu cudów.
48 Ngati ife timuleka kuti apitirize chotere, aliyense adzamukhulupirira Iye, ndipo kenaka Aroma adzabwera ndi kudzatenga malo athu pamodzi ndi dziko lathu.”
Jeżeli nic z nim nie zrobimy, wszyscy Mu uwierzą! A wtedy nadciągną Rzymianie i odbiorą nam świątynię i władzę nad krajem.
49 Kenaka mmodzi wa iwo, dzina lake Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe chaka chimenecho, anayankhula kuti, “Inu simukudziwa kanthu kalikonse!
W tym momencie głos zabrał niejaki Kajfasz, który tego roku sprawował urząd najwyższego kapłana: —Nic nie rozumiecie!
50 Inu simukuzindikira kuti kuli bwino kwa inu kuti munthu mmodzi afe mʼmalo mwa anthu kusiyana ndi kuti mtundu wonse uwonongeke.”
Przecież lepiej będzie, jeśli jeden człowiek umrze za naród, niż miałby zginąć cały naród.
51 Iye sananene izi mwa iye yekha, koma monga mkulu wa ansembe chaka chimenecho ananenera kuti Yesu anayanera kufera mtundu wa Ayuda,
Nie powiedział tego sam od siebie. Jako najwyższy kapłan wypowiedział proroctwo, że Jezus ma umrzeć za cały naród.
52 ndipo osati mtundu okhawo komanso kwa ana ena a Mulungu onse obalalikana, kuti awabweretse pamodzi ndi kuwapanga kukhala amodzi.
I nie tylko za naród, lecz również po to, aby zgromadzić razem wszystkie Boże dzieci rozproszone po świecie.
53 Choncho kuyambira tsiku limeneli iwo anakonzekera za kuti amuphe.
Tego dnia przywódcy postanowili więc, że zabiją Jezusa.
54 Chifukwa cha ichi Yesu sanayendenso moonekera pakati pa Ayuda. Mʼmalo mwake Iye anapita ku chigawo cha kufupi ndi chipululu, ku mudzi wa Efereimu, kumene Iye anakhalako ndi ophunzira ake.
Dlatego przestał On jawnie poruszać się po Judei. Skierował się natomiast wraz z uczniami do Efraim, miasteczka położonego blisko pustyni, i tam się zatrzymał.
55 Nthawi ya Paska wa Ayuda itayandikira, ambiri anakwera kupita ku Yerusalemu kuchokera ku madera a ku midzi chifukwa cha mwambo wa kuyeretsedwa Paska asanafike.
Zbliżało się właśnie święto Paschy. I mnóstwo ludzi z całego kraju napływało do Jerozolimy jeszcze przed świętem, aby dopełnić ceremonii oczyszczenia.
56 Iwo anapitiriza kumufunafuna Yesu, ndipo pamene ankayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi ukuganiza chiyani? Kodi Iye sabwera konse kuphwando?”
Wszyscy wypatrywali także Jezusa i będąc w świątyni pytali siebie nawzajem: —Jak myślicie, czy przyjdzie na uroczystości?
57 Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anapereka lamulo kuti ngati wina aliyense adziwe kumene kunali Yesu, iye akawawuze kuti akamugwire.
Najwyżsi kapłani i faryzeusze publicznie ogłosili wtedy, że każdy, kto zobaczy Jezusa, ma ich natychmiast o tym poinformować, aby można Go było aresztować.