< Yohane 10 >

1 “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani inu Afarisi, kuti munthu amene salowera pa khomo mʼkhola la nkhosa, koma amalowera pena pake ndi wakuba ndi wachifwamba.
Ikumbya line, nimiwambila, iye mwine yaseti enjile chamulyango wamulaka wembelele, kono utata kwiwulu chenzila imwi, unzo muntu musa mi wiba.
2 Munthu amene amalowera pa khomo ndi mʼbusa wankhosazo.
Iye winjilila kumulyango nji mulisana wembelele.
3 Mlonda amamutsekulira khomo, ndipo nkhosa zimamvera mawu ake. Iye amaziyitana mayina nkhosa zakezo, nazitulutsa.
Mubabaleli wamulyango mwamwiyalwile. Imbelele zizuwa inzwi lyakwe, mi usupa imbelele zakwe chamazina ni kuzietelela hazizwa.
4 Akazitulutsa nkhosa zake zonse, iye amazitsogolera, ndipo nkhosa zakezo zimamutsata chifukwa zimadziwa mawu ake.
Linu heti chazizwisa nzose zakwe, uziyenda kubusu, mi imbelele zimwichilila, mukuti zinzi inzwi lyakwe.
5 Koma nkhosazo sizidzatsatira mlendo. Izo zidzamuthawa chifukwa sizizindikira mawu a mlendo.”
Linu keti nizichilile muyenzi, kono kazimukekuluhe, mokuti kanzinzi inzwi lyamuyenzi.”
6 Yesu ananena mawu ophiphiritsawa, koma Afarisi sanazindikire zimene ankawawuza.
Jesu abawambi iyi nguli kubali, kono abo kanababazuwisisi kuti izi zintu ibali nji zona zabali kuwamba kubali.
7 Choncho Yesu anatinso, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Ine ndine khomo la nkhosa.
Linu Jesu chawamba kubali hape, Ikumbya line, Nimi wambila, Njime nimulyango wembelele.
8 Onse amene anadza ndisanabwere Ine ndi akuba ndi achifwamba, ndipo nkhosa sizinawamvere.
Yese yabezi kumasule angu musa mi wiba, kono imbelele kena zibamuteki.
9 Ine ndine khomo, aliyense amene alowa kudzera mwa Ine adzapulumuka. Iye adzalowa ndi kutuluka ndi kupeza msipu.
Njime nimulyango. Yese winjila changu, kapuluswe; kenjile mukati ni hanze mi kawane malisikizo.
10 Mbala sibwera chabe koma kuti idzabe, kupha ndi kuwononga. Ine ndabwera kuti iwo akhale ndi moyo, ndi kukhala nawo wochuluka.
Musa kawoli kwiza heba kezi kwiba kapa kwihaya ni kushinya. Nibakezi kuti benze bawane buhalo mi babu wane cha bungi.
11 “Ine ndine Mʼbusa wabwino. Mʼbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake.
Njime nimulisana weniti. Mulisana weniti uha buhalo bwakwe muchibaka chembelele.
12 Wantchito ndi mʼbusa amene nkhosazo si zake. Choncho, pamene aona mmbulu ukubwera, iye amazisiya nkhosazo ndi kuthawa. Ndipo mmbulu umagwira nkhosazo ndikuzibalalitsa.
Mubeleki wakuhila kahena mulisana wembelele imi kamunite imbelele. Habona untuhu nakezite usiya imbelele ni kubaleha. Utuhu uwonda imbelele ni kuzihasanya.
13 Munthuyo amathawa chifukwa ndi wantchito ndipo sasamalira chilichonse cha nkhosazo.
Utiya mukuti mubeleki wakuhila kabileli ni mbelele.
14 “Ine ndine mʼbusa wabwino. Ine ndimazidziwa nkhosa zanga ndipo nkhosa zangazo zimandidziwa,
Njime ni mulisani weniti, imi nizi zangu, mi zangu zinizi.
15 monga momwe Atate amandidziwa Ine, ndiponso Ine kudziwira Atatewo. Ndimapereka moyo wanga chifukwa cha nkhosa.
Tayo unizi, imi name nizi Tayo, imi nibahi buhalo bwangu muchibaka che mbelele.
16 Ine ndili ndi nkhosa zina zimene sizili za gulu ili. Ine ndiyenera kuzibweretsanso. Izonso zidzamvera mawu anga, ndipo zidzakhala gulu limodzi ndi mʼbusa mmodzi.
Nina imbelele zimwi zisali nzowo mulaka wembelele. Niyelele kuzileta nazo, imi kazizuwe inzwi lyangu kokuti ibe mutapi wonke ni mulisana yenke.
17 Nʼchifukwa chake Atate anga amandikonda, popeza Ine ndikupereka moyo wanga kuti ndiwutengenso.
Njikeli ibaka Tayo hanisaka: Nisinyehelwa buhalo bwangu kokuti ninibuhinde hape.
18 Palibe amene angawuchotse mwa Ine, koma ndikuwupereka mwakufuna kwanga. Ine ndili ndi ulamuliro wa kuwupereka ndi ulamuliro wakuwutenganso. Lamulo ili ndinalandira kwa Atate anga.”
Kakwina yowola kubuninyanga, kono nibusinyehelwa changu nimwine. Nina maata akuzwisa, imi nina maata akuhinda hape. Nibawani iyo itaelo kuba Tayo.
19 Pa mawu awa Ayuda anagawikananso.
Kuliyabahakati chikwa tendahala mukati kaMajuda bakeñisa chayo manzwi.
20 Ambiri a iwo anati, “Iye ndi wogwidwa ndi ziwanda ndi wamisala. Chifukwa chiyani mukumvera Iye?”
Bungi bwabo chiba wamba, “Wina i dimona mi umbulumuka. Chinzi hamutekeleza kwali?
21 Koma ena anati, “Awa si mawu a munthu wogwidwa ndi ziwanda. Kodi ziwanda zingathe bwanji kutsekula maso a wosaona?”
Bamwi chibati, “Aa kahena manzwi amuntu yoyendiswa idimona. Kana idimona liwola kwiyalula menso amuntu yasaboni?”
22 Ku Yerusalemu kunali chikondwerero chokumbukira kupatulidwa kwa Nyumba ya Mulungu. Inali nthawi yozizira,
Linu chibali inako ya Mukiti wa Kunjoloza mwa Jerusalema.
23 ndipo Yesu ankayenda mʼbwalo la Nyumbayo ku malo a Solomoni.
Ibali maliha, mi Jesu abu kuyenda mwi keleke mumalibela a Solomoni.
24 Ayuda anamuzungulira Iye akunena kuti, “Kodi iwe udzazunguza malingaliro athu mpaka liti? Ngati iwe ndi Khristu, tiwuze momveka.”
Linu Majuda chiba muzimbuluka mi chiba wamba kwali, katuhinde inako ikumahi nitu sezibi? Heba njiwe Kirisite, tuwambile he ñandaleza.”
25 Yesu anayankha kuti, “Ine ndimakuwuzani, koma inu simukhulupirira. Ntchito zimene ndikuchita mʼdzina la Atate anga zikundichitira umboni,
Jesu ababetabi kuti, “Nibamiwambili, kono kamuzumini. Mitendo initenda mwizina lya Tayo, yeyo njiipaka ziniama.
26 koma inu simukhulupirira chifukwa simuli a gulu lankhosa zanga.
Nikwinabulyo inwe ka muzumini mukuti kahena mwimbelele zangu.
27 Nkhosa zanga zimamva mawu anga, Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsata Ine.
Imbelele zangu zizuwa inzwi lyangu; nizizi, imi zinichilila.
28 Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. (aiōn g165, aiōnios g166)
Niziha buhalo busamani; kesinizifwe, imi kakwina niumwina yetinazi nzwabule mumayaza angu. (aiōn g165, aiōnios g166)
29 Atate anga, amene anandipatsa Ine, ndi akulu kuposa onse. Palibe amene angazikwatule mʼdzanja la Atate anga.
Tayo, yabazinihi, mukando kuzamba bonse, mi kakwina yowola kubazwabula mumayaza a Tayo.
30 Ine ndi Atate ndife amodzi.”
Ime ni Tayo tuchintu chonke.”
31 Ayuda anatolanso miyala kuti amugende Iye,
Linu Majuda chi bahinda mavwe nibamu ñabola.
32 koma Yesu anawawuza kuti, “Ine ndakuonetsani zinthu zambiri zabwino zodabwitsa kuchokera kwa Atate. Nʼchifukwa chiti mwa izi chimene mukundigendera?”
Jesu ababetabi, “Nibamitondezi mitendo mingi milotu izwa kwa Tayo. Linu njo uhi kweyo mitendo umuniñabolela cha mabwe?”
33 Ayuda anayankha kuti, “Ife sitikukugenda chifukwa cha izi, koma popeza ukunyoza Mulungu, chifukwa iwe, munthu wamba, ukuti ndiwe Mulungu.”
Majuda babamwitabi, “Katuku ñaboleli mutendo mulotu, kono kushwaula, mukuti iwe, umuntu, uli tenda kuti njowe Ireeza.”
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi sizinalembedwa mʼmalamulo anu kuti, ‘Ine ndanena kuti ndinu milungu?’
Jesu ababetabi, “Kanakuti kuñoletwe mumilao, Ni wamba, “mumizimu”?
35 Ngati anawatcha milungu anthu amene analandira mawu a Mulungu, pajatu Malemba sangasweke,
Heba ababa supi kuti bazimu, nji kwani kulibazwi izina lya Ireeza (mi mañolo ka awoli ku lutwa),
36 nanga bwanji uyu amene Atate anamuyika padera monga wake weniweni ndi kumutuma ku dziko lapansi? Nanga ndi chifukwa chiyani mukundinena Ine kuti ndikuchita chipongwe? Kodi nʼchifukwa choti ndanena kuti, ‘Ine ndine Mwana wa Mulungu?’
muwamba konzo yaba bikiwakumbali nji Tayo ni kutumiwa muchisi, 'ushwaula; mukuti na wamba, 'Ni mwana we Ireeza.'
37 Musandikhulupirire Ine ngati sindichita ntchito za Atate anga.
Heba kanitendi mitendo ya Tayo, kanzi muni zumini.
38 Koma ngati Ine ndikuchita zimenezi, ngakhale kuti simundikhulupirira, khulupirirani ntchito zodabwitsazo, ndipo mudziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndiponso Ine ndili mwa Atate.”
Kono heba niitenda, nangakuti kazumini, muzumine mitendo linukuti mwizimbe ni kuzuwisisa ziba Tayo benamwangu imi name ninamuba Tayo.”
39 Iwo anafuna kumugwiranso koma anawapulumuka mʼmanja mwawo.
Babaliki kumuwonda hape, kono abayindi kungi kuzwa mumayanza abo.
40 Kenaka Yesu anabwereranso kutsidya la mtsinje wa Yorodani kumalo kumene Yohane ankabatiza mʼmasiku akale. Iye anakhala kumeneko
Chayenda hape mwishila lya Jorodani kuchibaka unko Joani abali kukolobeza, niku kekala kwateni.
41 ndipo anthu ambiri anabwera kwa Iye. Iwo anati, “Ngakhale kuti Yohane sanachite chizindikiro chodabwitsa, zonse zimene Yohane ananena za munthu uyu zinali zoona.”
Bungi bwabantu chibeza kwali nikuchokuti, “Cheniti Joani kana abatendi imakazo, kono zintu zonse zaba wambi Joani chozu mukwame ibali zeniti.”
42 Ndipo pamalo amenewo ambiri anakhulupirira Yesu.
Bantu bangi kwateni ni chibazumina kwali.

< Yohane 10 >