< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
The Lord’s message that came to Joel, son of Pethuel.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hear this, elders, pay attention, all inhabitants of the land. Has anything like this happened in your days, or in the days of your ancestors?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Recount it to your children; let your children tell it to their children, and their children to the generation that follows.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
That which the cutting locust has left, the swarming locust has eaten, that which the swarming locust has left, the hopping locust has eaten, and that which the hopping locust has left, the destroying locust has eaten.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Awake, drunkards, and weep, and wail, all drinkers of wine; the new wine is cut off from your mouth.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For a nation has come up on my land, powerful, and numberless; its teeth are the teeth of a lion, and its jaw-teeth are like those of a lioness.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
It has laid waste my vines, and barked my fig tree; it has peeled and cast it away, bleached are the branches.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Wail as a bride, clad in sack-cloth, for the husband of her youth.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
Cut off are the cereal and drink-offerings from the house of the Lord; in mourning are the priests, who minister at the Lord’s altar.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
The fields are blasted, the land is in mourning, for ruined is the grain, the new wine fails and the oil is dried up.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Be dismayed, farmers; wail, vine-dressers. For the wheat and the barley; for the harvest is lost from the fields.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vine fails to bear fruit, and the fig tree is drooping; the pomegranate, palm, and apple, all the trees of the field are dried up. The people’s joy withers.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Put on sackcloth, and beat your breasts, priests; wail, ministers of the altar; come, lie all night in sack-cloth, ministers of God; for cereal-offering and drink-offering are cut off from the house of your God.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Sanctify a fast, summon an assembly, gather the elders and all the inhabitants of the land into the house of the Lord your God, cry to the Lord:
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Alas for the day! Near at hand is the day of the Lord, and as destruction from the Almighty it comes.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Is not food cut off from before us, gladness and joy from the house of our God?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
The grains shrivel under their hoes, the storehouses are desolate, the barns broken down, for the grain is withered.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
How the herds of cattle bellow in distress, for they have no pasture! The flocks of sheep are forlorn.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
To you, the Lord, I cry. For fire has devoured the pastures of the wilderness, and flame has scorched all the trees of the field.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
The wild animals also look up to you longingly, for the water-courses are dried up, and fire has devoured the pastures of the wilderness.

< Yoweli 1 >