< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
The word of the Lord which came to Joel the son of Bathuel.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hear these [words], ye elders, and hearken all ye that inhabit the land. Have such things happen in your days, or in the days of your fathers?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Tell your children concerning them, and [let] your children [tell] their children, and their children another generation.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
The leavings of the caterpillar has the locust eaten, and the leavings of the locust has the palmerworm eaten, and the leavings of the palmerworm has the cankerworm eaten.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Awake, ye drunkards, from your wine, and weep: mourn, all ye that drink wine to drunkenness: for joy and gladness and removed are from your mouth.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For a strong and innumerable nation is come up against my land, their teeth are lion's teeth, and their back teeth those of a [lion's] whelp.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
He has ruined my vine, and utterly broken my fig-trees: he has utterly searched [my vine], and cast it down; he has peeled its branches.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Lament to me more than a virgin girded with sackcloth for the husband of her youth.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
The meat-offering and drink-offering are removed from the house of the Lord: mourn, ye priests that serve at the altar of the Lord.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
For the plains languish: let the land mourn, for the corn languishes; the wine is dried up, the oil becomes scarce;
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
the husbandmen are consumed: mourn your property on account of the wheat and barley; for the harvest has perished from off the field.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vine is dried up, and the fig-trees are become few; the pomegranate, and palm-tree, and apple, and all trees of the field are dried up: for the sons of men have have abolished joy.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Gird yourselves [with sackcloth], and lament, ye priests: mourn, ye that serve at the altar: go in, sleep in sackcloths, ye that minister to God: for the meat-offering and drink-offering are withheld from the house of your God.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Sanctify a fast, proclaim a [solemn] service, gather the elders [and] all the inhabitants of the land into the house of your God, and cry earnestly to the Lord,
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Alas, Alas, Alas for the day! for the day of the Lord is nigh, and it will come as trouble upon trouble.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
[Your] meat has been destroyed before your eyes, joy and gladness from out of the house of your God.
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
The heifers have started at their mangers, the treasures are abolished, the wine-presses are broken down; for the corn is withered.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
What shall we store up for ourselves? the herds of cattle have mourned, because they had no pasture; and the flocks of sheep have been utterly destroyed.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
To thee, O Lord, will I cry: for fire has devoured the fair places of the wilderness, and a flame has burnt up all the trees of the field.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
And the cattle of the field have looked up to thee: for the fountains of waters have been dried up, and fire has devoured the fair places of the wilderness.

< Yoweli 1 >