< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
上主的話傳給培特耳的兒子岳厄爾:
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
老人們,你們應聽這事! 地上的一切在你們的應側耳細聽! 在你們的時日,或在你們的祖先的時日,是否有過這樣的事﹖
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
你們應將這樣的事告訴你們的子孫,你們的子孫應傳給你們的的子孫;他們的子孫又應代傳給下一代:
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
蝻子吃剩的,飛蝗來吃了;飛蝗吃剩的,冬斯來吃了;冬斯吃剩的,蚱蜢來吃了。
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
醉漢,你們醒來慟哭吧! 一切愛暍酒的人,為了新酒悲泣吧! 因為已由你們嘴邊奪去了。
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
因為有一個民族侵入了我的地區,既強大而又不可勝數;你們的牙猶如獅子的牙,臼齒有如母獅的臼齒。
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
他們蹂躝了我的葡萄園,折斷了我的無花果樹,將樹皮完全剝掉,使樹枝光禿發白。
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
你哀傷吧! 如同一個身披喪服的處女,哀哭她青年的未婚夫。
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
上主殿中的素祭和奠祭已中斷;上主的僕人──司祭都都悲哀不已。
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
田園已荒廢,土地已淒涼;因為五榖已遭蹂躝,美酒已枯竭,油已乾涸。
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
農夫,你們應哀哭! 葡萄園丁,你們應為小麥和大麥而號咷! 因為田園的出產已遭。破壞
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
葡萄樹枯槁了,無花果樹凋謝了;石榴樹、棕樹、蘋果樹,以及田間大中的一切果樹都枯死了;為此,喜樂已由人間消失。
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
司祭,你們應披上麻衣而哀悼! 服務祭壇的人,你們應號咷! 我天主的僕人,你們應進來,披上麻衣過夜! 因為素祭和奠祭在你們天主的殿內已中斷了。
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
你們應制定一個齋期,召開一個盛會,聚集長老和當地的一切居民,在上主你們的天主的殿內,向上主呼號o
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
那日子啊! 上主的日子來近了,它來有如全能者施行毀滅。
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
食物不是在我們眼斷絕了嗎﹖喜樂和歡欣不是離開了我們天主的殿嗎﹖
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
麥粒已在土塊下腐爛,糧倉業已荒廢,廩倉業已坍塌,因為五榖都枯死了。
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
牲畜為什麼悲鳴﹖牛群為什麼徬徨﹖因為沒有了草場;連群也感絕望。
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
上主,我向你呼號,因為烈火吞滅了原野的牧場,火燄焚燒了田間的一切樹木。
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
連野獸也向你懇切哀鳴,因為水流已枯竭,烈火又吞滅了原野的牧場。

< Yoweli 1 >