< Yoweli 3 >

1 “Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
Кэч ятэ кэ, ын зилеле ачеля ши ын времуриле ачеля кынд вой адуче ынапой пе принший де рэзбой ай луй Иуда ши ай Иерусалимулуй,
2 ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
вой стрынӂе пе тоате нямуриле ши ле вой коборы ын Валя луй Иосафат. Аколо, Мэ вой жудека ку еле пентру попорул Меу, пентру Исраел, моштениря Мя, пе каре л-ау рисипит принтре нямурь, ымпэрцинд ынтре еле цара Мя.
3 Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
Ау трас ла сорць пентру попорул Меу; ау дат ун флэкэу пе о курвэ ши ау вындут фата пе вин ши л-ау бэут.
4 “Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
Че врець вой ку Мине, Тируле ши Сидонуле ши тоате цинутуриле филистенилор? Врець сэ-Мь рэсплэтиць врео фаптэ сау сэ фачець чева ымпотрива Мя? Юте, фэрэ зэбавэ, вой ынтоарче фаптеле воастре асупра капулуй востру.
5 Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
Мь-аць луат арӂинтул ши аурул ши челе май буне одоаре але Меле ши ле-аць дус ын темплеле воастре.
6 Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
Аць вындут пе копиий луй Иуда ши ай Иерусалимулуй копиилор гречилор, ка сэ-й депэртаць дин цара лор.
7 “Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
Ятэ кэ ый скол ын локул ын каре й-аць вындут ши вой ынтоарче фапта воастрэ асупра капулуй востру.
8 Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
Вой винде копиилор луй Иуда пе фиий ши фийчеле воастре, ши ей ый вор винде сабеенилор, ун ням депэртат, кэч Домнул а ворбит.”
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
Вестиць ачесте лукрурь принтре нямурь: „Прегэтиць рэзбоюл! Трезиць пе витежь! Сэ се апропие ши сэ се суе тоць оамений де рэзбой!
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
Фяреле плугурилор воастре префачеци-ле ын сэбий ши косоареле, ын сулице! Чел слаб сэ зикэ: ‘Сунт таре!’”
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
Грэбици-вэ ши вениць, тоате нямуриле де примпрежур, ши стрынӂеци-вэ! Аколо кобоарэ, Доамне, пе витежий Тэй!
12 “Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
„Сэ се скоале нямуриле ши сэ се суе ын Валя луй Иосафат! Кэч аколо вой шедя сэ жудек тоате нямуриле де примпрежур.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
Пунець мына пе сечерэ, кэч сечеришул есте копт! Вениць ши кэлкаць ку пичоареле, кэч линуриле сунт плине ши точиториле дау песте еле! Кэч маре есте рэутатя лор!”
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
Вин грэмезь-грэмезь ын валя жудекэций, кэч зиуа Домнулуй есте апроапе, ын валя жудекэций.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
Соареле ши луна се ынтунекэ ши стелеле ышь перд стрэлучиря.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
Домнул рэкнеште дин Сион, гласул Луй рэсунэ дин Иерусалим де се згудуе черуриле ши пэмынтул. Дар Домнул есте скэпаря попорулуй Сэу ши окротиря копиилор луй Исраел.
17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
„Ши вець шти кэ Еу сунт Домнул Думнезеул востру, каре локуеште ын Сион, мунтеле Меу чел сфынт. Иерусалимул ынсэ ва фи сфынт ши ну вор май трече стрэиний прин ел.
18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
Ын время ачея, ва пикура муст дин мунць ши ва курӂе лапте дин дялурь, тоате пыраеле луй Иуда вор фи плине де апэ. Ун извор ва еши, де асеменя, дин Каса Домнулуй ши ва уда валя Ситим.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
Еӂиптул ва ажунӂе пустиу, Едомул ва ажунӂе ун пустиу стерп дин причина силничией фэкуте ымпотрива копиилор луй Иуда, ал кэрор сынӂе невиноват л-ау вэрсат ын цара лор.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
Дар Иуда ва фи вешник локуит ши Иерусалимул, дин ням ын ням.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”
Ле вой рэзбуна сынӂеле пе каре ну л-ам рэзбунат ынкэ, дар Домнул ва локуи ын Сион.”

< Yoweli 3 >