< Yoweli 3 >
1 “Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
Oto bowiem w tych dniach i w tym czasie, gdy odwrócę niewolę ludu Judy i Jerozolimy;
2 ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
Zgromadzę też wszystkie narody i sprowadzę je do Doliny Jehoszafata, i będę tam z nimi rozprawiał o swoim ludzie i o swoim dziedzictwie Izraela, które rozproszyły wśród narodów i podzieliły moją ziemię.
3 Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
O mój lud rzucały los, dawały chłopca za nierządnicę i dziewczynę sprzedawały za wino, aby piły.
4 “Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
Ale wy cóż macie przeciwko mnie, Tyrze i Sydonie, oraz wszystkie granice filistyńskie? Czy chcecie dać mi odpłatę? Jeśli mi odpłacicie, to prędko i niezwłocznie i ja zwrócę waszą odpłatę na waszą głowę;
5 Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
Gdyż zabraliście moje srebro i złoto, a moje wspaniałe klejnoty wnieśliście do swoich świątyń;
6 Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
A synów Judy i synów Jerozolimy sprzedaliście Grekom, by ich oddalić od ich granic.
7 “Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
Oto wzbudzę ich z tego miejsca, do którego ich sprzedaliście, i zwrócę waszą zapłatę na waszą głowę;
8 Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
I sprzedam waszych synów i wasze córki w ręce synów Judy, a oni sprzedadzą ich Sabejczykom, narodowi dalekiemu. Tak bowiem PAN powiedział.
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
Rozgłoście to wśród pogan, ogłoście wojnę, pobudźcie wojowników, niech przybędą [i] niech wyruszą wszyscy mężowie waleczni.
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
Przekujcie wasze lemiesze na miecze, a wasze sierpy na oszczepy; kto słaby, niech powie: Jestem silny.
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
Zgromadźcie się i przyjdźcie, wszystkie okoliczne narody – zbierzcie się. Sprowadź tam, PANIE, swoich wojowników.
12 “Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
Niech poganie się ockną i nadciągną na Dolinę Jehoszafata. Tam bowiem zasiądę, aby sądzić wszystkie okoliczne narody.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
Zapuśćcie sierp, bo dojrzało żniwo. Pójdźcie i zstąpcie, bo tłocznia jest pełna, kadzie przelewają się, bo ich zło [jest] wielkie.
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
Tłumy, tłumy w dolinie wyroku. Bliski bowiem jest dzień PANA w dolinie wyroku.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
Słońce i księżyc się zaćmią i gwiazdy stracą swój blask.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
I PAN zagrzmi z Syjonu, a z Jerozolimy wyda swój głos, tak że zadrżą niebiosa i ziemia. Ale PAN będzie ucieczką dla swego ludu i siłą synów Izraela.
17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
I poznacie, że ja jestem PANEM, waszym Bogiem, który mieszka na Syjonie, mojej świętej górze. I Jerozolima stanie się święta, a obcy już nie będą przez nią przechodzić.
18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
I stanie się w tym dniu, że góry będą kropić moszczem, pagórki opływać mlekiem i wszystkie strumienie Judy napełnią się wodą, a z domu PANA wyjdzie źródło, które nawodni dolinę Sittim.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
Egipt zostanie spustoszony, a ziemia Edom zamieni się w opustoszałe pustkowie z powodu przemocy wyrządzonej synom Judy, bo przelewali niewinną krew w ich ziemi.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
Ale Juda będzie trwać na wieki, a Jerozolima – z pokolenia na pokolenie.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”
I oczyszczę tych, [których] krwi nie oczyściłem. PAN bowiem mieszka na Syjonie.