< Yoweli 3 >
1 “Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
« Car voici, en ces jours-là, et pendant ce temps, quand je restaurerai la fortune de Juda et de Jérusalem,
2 ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
Je rassemblerai toutes les nations, et les fera descendre dans la vallée de Josaphat; et je les jugerai là-bas, pour mon peuple, et pour mon héritage, Israël, qu'ils ont dispersé parmi les nations. Ils ont divisé mes terres,
3 Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
et j'ai tiré au sort mon peuple, et ont donné un garçon pour une prostituée, et vendu une fille pour du vin, afin qu'ils puissent boire.
4 “Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
« Oui, et qu'êtes-vous pour moi, Tyr et Sidon, et toutes les régions de la Philistie? Vous me rembourserez? Et si vous me remboursez, Je vous renverrai rapidement et promptement votre remboursement sur votre propre tête.
5 Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
Parce que tu as pris mon argent et mon or, et ont transporté mes plus beaux trésors dans vos temples,
6 Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
et ils ont vendu les enfants de Juda et les enfants de Jérusalem aux fils des Grecs, afin que tu les éloignes de leur frontière.
7 “Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
Voici, je vais les faire sortir du lieu où vous les avez vendus, et vous rendrez votre remboursement sur votre propre tête;
8 Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
et je vendrai tes fils et tes filles entre les mains des enfants de Juda, et ils les vendront aux hommes de Saba, à une nation lointaine, car Yahvé l'a dit. »
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
Proclamez ceci parmi les nations: « Préparez-vous à la guerre! Réveillez les hommes forts. Que tous les guerriers s'approchent. Laissez-les monter.
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
Transformez vos socs en épées, et vos crochets d'élagage en lances. Que le faible dise: « Je suis fort.
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
Dépêchez-vous et venez, vous toutes les nations environnantes, et rassemblez-vous. » Fais descendre tes puissants, Yahvé.
12 “Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
« Que les nations se réveillent! et de monter dans la vallée de Josaphat; car c'est là que je m'assiérai pour juger toutes les nations environnantes.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
Mettez la faucille; car la récolte est mûre. Venez, foulez, car le pressoir est plein, les cuves débordent, car leur méchanceté est grande. »
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
Des multitudes, des multitudes dans la vallée de la décision! Car le jour de Yahvé est proche dans la vallée de la décision.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
Le soleil et la lune sont obscurcis, et les étoiles retirent leur éclat.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
De Sion, Yahvé rugira, et le tonnerre de Jérusalem; et les cieux et la terre trembleront; mais Yahvé sera un refuge pour son peuple, et une forteresse pour les enfants d'Israël.
17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
« Ainsi, vous saurez que je suis Yahvé, votre Dieu, qui habite à Sion, ma montagne sainte. Alors Jérusalem sera sainte, et aucun étranger ne passera plus par elle.
18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
Cela arrivera en ce jour-là, que les montagnes laisseront tomber du vin doux, les collines couleront de lait, tous les ruisseaux de Juda couleront avec des eaux; et une fontaine jaillira de la maison de Yahvé, et arrosera la vallée de Shittim.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
L'Égypte sera une désolation et Edom sera un désert, pour les violences faites aux enfants de Juda, parce qu'ils ont versé du sang innocent dans leur pays.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
Mais Juda sera habité pour toujours, et Jérusalem de génération en génération.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”
Je purifierai leur sang que je n'ai pas purifié, car Yahvé habite en Sion. »