< Yoweli 3 >
1 “Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
For behold, in those days and at that time, When I shall bring back the captives of Judah and Jerusalem,
2 ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
I will assemble all the nations, And will bring them down it to the valley of Jehoshaphat, And there will I contend with them for my people and inheritance, Israel; Because they scattered them among the nations, And divided my land among themselves.
3 Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
Yea, they cast lots for my people, And gave a boy for a harlot, And sold a damsel for wine to drink.
4 “Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
What have ye to do with me, O Tyre and Sidon, And all the borders of Philistia? Will ye retaliate on me? Or will ye do anything against me? Swiftly and speedily will I bring back your doings upon your own head.
5 Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
Ye have taken my silver and my gold, And have carried into your palaces my precious, goodly things;
6 Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
The sons also of Judah, and the sons of Jerusalem, Ye have sold to the Grecians, That ye might remove them far from their border.
7 “Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
Behold, I will raise them out of the place whither ye have sold them, And I will return your injury upon your own head;
8 Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
I will sell your sons and your daughters into the hand of the sons of Judah, And they shall sell them to the Sabeans, to a nation afar off; For Jehovah hath spoken it.
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
Proclaim ye this among the nations: “Prepare war! Stir up the mighty ones! Let all the warriors draw near; let them come up!”
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
Beat your ploughshares into swords, And your pruning-hooks into spears; Let the weak say, I am strong!
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
Assemble yourselves and come, all ye nations round about; Gather yourselves together! Thither, O Jehovah, bring down thy mighty ones!
12 “Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
Let the nations rise and come up to the valley of Jehoshaphat! For there will I sit to judge all the nations around.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
Put ye in the sickle, for the harvest is ripe; Come and tread, for the wine-press is full; The vats overflow; For their wickedness is great!
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
The multitudes, the multitudes in the valley of judgment! For the day of Jehovah is near in the valley of judgment.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
The sun and the moon are darkened, And the stars withdraw their shining.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
Jehovah also will roar from Zion, And utter his voice from Jerusalem; The heavens and the earth shall shake. But Jehovah will be a refuge to his people! A strong-hold to the sons of Israel.
17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
Then shall ye know that I am Jehovah your God, Dwelling in Zion, my holy mountain; And Jerusalem shall be holy; Strangers shall pass through her no more.
18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
In that day shall the mountains drop down new wine, And the hills shall flow with milk. And all the streams of Judah shall flow with water. A fountain shall come forth from the house of Jehovah, That shall water the valley of Shittim.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
Egypt shall be a waste, And Edom a desolate wilderness, For their violence against the sons of Judah; For they shed innocent blood in their land.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
But Judah shall be inhabited for ever, And Jerusalem from generation to generation.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”
And I will avenge their blood, which I have not avenged, And Jehovah will dwell upon Zion.