< Yoweli 3 >
1 “Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
For behold in those days, and in that time when I shall bring back the captivity of Juda and Jerusalem:
2 ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
I will gather together all nations, and will bring them down into the valley of Josaphat: and I will plead with them there for my people, and for my inheritance Israel, whom they have scattered among the nations, and have parted my land.
3 Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
And they have cast lots upon my people: and the boy they have put in the stews, and the girl they have sold for wine, that they might drink.
4 “Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
But what have you to do with me, O Tyre, and Sidon, and all the coast of the Philistines? will you revenge yourselves on me? and if you revenge yourselves on me, I will very soon return you a recompense upon your own head.
5 Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
For you have taken away my silver and my gold: and my desirable and most beautiful things you have carried into your temples.
6 Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
And the children of Juda, and the children of Jerusalem you have sold to the children of the Greeks, that you might remove them far off from their own country.
7 “Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
Behold, I will raise them up out of the place wherein you have sold them: and I will return your recompense upon your own heads.
8 Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
And I will sell your sons, and your daughters by the hands of the children of Juda, and they shall sell them to the Sabeans, a nation far off, for the Lord hath spoken it.
9 Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
Proclaim ye this among the nations: prepare war, rouse up the strong: let them come, let all the men of war come up.
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
Cut your ploughshares into swords, and your spades into spears. Let the weak say: I am strong.
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
Break forth, and come, all ye nations, from round about, and gather yourselves together: there will the Lord cause all thy strong ones to fall down.
12 “Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
Let them arise, and let the nations come up into the valley of Josaphat: for there I will sit to judge all nations round about.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
Put ye in the sickles, for the harvest is ripe: come and go down, for the press is full, the fats run over: for their wickedness is multiplied.
14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
Nations, nations in the valley of destruction: for the day of the Lord is near in the valley of destruction.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
The sun and the moon are darkened, and the stars have withdrawn their shining.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
And the Lord shall roar out of Sion, and utter his voice from Jerusalem: and the heavens and the earth shall be moved, and the Lord shall be the hope of his people, and the strength of the children of Israel.
17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
And you shall know that I am the Lord your God, dwelling in Sion my holy mountain: and Jerusalem shall be holy and strangers shall pass through it no more.
18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
And it shall come to pass in that day, that the mountains shall drop down sweetness, and the hills shall flow with milk: and waters shall flow through all the rivers of Juda: and a fountain shall come forth of the house of the Lord, and shall water the torrent of thorns.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
Egypt shall be a desolation, and Edom a wilderness destroyed: because they have done unjustly against the children of Juda, and have shed innocent blood in their land.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
And Judea shall be inhabited for ever, and Jerusalem to generation and generation.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”
And I will cleanse their blood which I had not cleansed: and the Lord will dwell in Sion.