< Yoweli 2 >
1 Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
Blow the trumpet in Zion! Sound the alarm on my holy mountain! Let all who live in the land tremble for the day of the Lord is coming—it's definitely near!
2 tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
It's a gloomy day of darkness, a day of thick clouds and heavy shadows. Like the dawn spreading over the mountains, an army appears, so large and powerful that there has never ever been anything like it before, nor will there ever be anything like it again.
3 Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
Fire blazes in front of them, behind them flames are burning. In front of them the land looks like the Garden of Eden, behind them is a desert of total desolation: not a single survivor remains.
4 Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
They have the appearance of horses; they charge like cavalry.
5 Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
Listen to the sound: they are like rumbling chariots leaping over the mountain tops, they are like crackling flames burning stubble, they are like a mighty army marching in formation into battle.
6 Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
Terror seizes all those in their path; all the people's faces grow pale.
7 Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
They attack like mighty warriors; they scale walls like soldiers. They all march as one, never breaking ranks.
8 Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
They do not jostle one another, they stay on track; and even if some are cut down, they are not stopped.
9 Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
They rush to and fro in the city; they run along the walls; they climb into houses, entering through the windows like thieves.
10 Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
The earth quakes before them, the heavens tremble, the sun and the moon grow dark, the stars stop shining.
11 Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
The Lord shouts his commands at the head of his army. His camp his immense, and those who carry out his orders are powerful. The day of the Lord is totally terrifying—who can stand it?
12 “Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
“Yet even now,” says the Lord, “Come back to me while there is still time. Come to me with all your heart, with fasting and prayer.
13 Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
Repent in your minds, and not by tearing your clothes.” Come back to the Lord your God for he is gracious and kind. He is slow to get angry and full of faithful love, and changes his mind about sending punishment.
14 Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
Who knows? Maybe he will change his mind, leaving behind a blessing so that you will be able to make grain and wine offerings to the Lord your God.
15 Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
Blow the trumpet in Zion! Proclaim a fast; call a solemn assembly.
16 Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
Gather the people together: the elders, the children, even the babies. Let the bridegroom leave his room; let the bride leave her room.
17 Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
Let the priests, the ministers of the Lord, weep between the porch and the altar of the Temple. Let them say, “Lord, please take pity on your people, and do not let your inheritance be disgraced, ruled over by foreign nations, so that the people of these nations could ask, ‘Where is their God?’”
18 Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
Now the Lord is very protective of his land and takes pity on his people.
19 Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
The Lord will reply, saying to his people, “Look! I am sending you grain and new wine and olive oil, and you will be satisfied. You will no longer be a disgrace among the foreign nations.
20 “Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
I will remove from you the army from the north; I will drive them into the desolate wilderness—the front into the eastern sea, and the rear into the western sea. The stench of the dead army will rise up—a real stink—for it has done terrible things.”
21 Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
Don't be afraid, people of the land! Be happy and celebrate, for the Lord has done incredible things!
22 Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
Don't be afraid, wild animals! For the pastures of the wilderness are turning green. The trees are fruiting again—the fig trees and the grapevines are producing a good crop.
23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
People of Jerusalem! Celebrate and be happy in the Lord your God because he has given you rain to show his goodness. As before he sends the autumn and the spring rains.
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
The threshing floors will be full of grain, the vats will overflow with new wine and olive oil.
25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
“I will give back to you what you lost over the years to the swarming, hopping, destroying, and cutting locusts, this great army that I sent against you.
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
You will have plenty to eat, and you will be satisfied, and you will praise the name of the Lord your God who has done miracles for you. My people will never again be ashamed.
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
You will know that I am in the midst of my people Israel, that I am the Lord your God, and that there is no other. My people will never again be ashamed.
28 “Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
After this I will pour out my spirit on everyone. Your sons and daughters will be my prophets, your old men will dream dreams, and your young men will see visions.
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
In those days I will also pour out my spirit on male slaves and female slaves.
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
I will place wonders in the heavens and on earth: blood, and fire, and columns of smoke.
31 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
The sun will turn dark, and the moon will turn red like blood at the coming of the great and fearful day of the Lord.”
32 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.
Then everyone who calls on the name of the Lord will be saved, rescued from Mount Zion and Jerusalem, as the Lord has said—these are among the survivors the Lord has called.