< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
Ilizwi likaThixo lafika kuJoweli indodana kaPhethuweli.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Zwanini lokhu, lina badala; lalelani lonke lina elihlala elizweni. Into enjengale seyake yenzakala na ensukwini zenu loba ensukwini zabokhokho benu?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Kutsheleni abantwabenu, abantwabenu labo batshele ababantwababo, abantwababo batshele isizukulwane esilandelayo.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
Lokho okutshiywe ngumtshitshi wezintethe kudliwe yisikhongwane; okutshiywe yisikhongwane kudliwe yibuyane; okutshiywe yibuyane kudliwe ngezinye intethe.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Vukani lina zidakwa likhale! Lilani lonke lina banathi bewayini; lilani ngenxa yewayini elitsha, ngoba lihluthunwe ezindebeni zenu.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
Isizwe sihlasele ilizwe lami, silamandla asingeke sibalwe, silamazinyo esilwane, ingavula zesilwanekazi.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
Sesitshabalalise izivini zami, saqothula lezihlahla zami zemikhiwa. Sebule amaxolo azo sawaphosela khatshana, ingatsha zazo zasala sezimhlophe nke.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Lilani njengentombi egqoke isaka idabukele umyeni wobutsha bayo.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
Umnikelo wamabele lomnikelo wokunathwa kususiwe endlini kaThixo. Abaphristi bayalila, bona abakhonzayo phambi kukaThixo.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
Amasimu atshabalele, umhlabathi womile; amabele onakele, iwayini elitsha liphelile, amafutha kawasekho.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Delani, lina balimi, lilani, lina balimi bamavini; bubulelani ingqoloyi lebhali, ngoba isivuno sensimu sitshabalalisiwe.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
Ivini lomile lomkhiwa ubunile; iphomegranathi, lelala lesihlahla sama-aphula, zonke izihlahla zeganga, zomile. Impela ukuthokoza kwabantu kuphelile.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Vunulani amasaka, lina baphristi, likhale. Lilani lina elikhonzayo phambi kwe-alithari. Wozani, lilale lembethe amasaka ebusuku, lina elikhonzayo phambi kukaNkulunkulu wami, ngoba iminikelo yamabele leminikelo yokunathwayo igodliwe, kayanikelwa endlini kaNkulunkulu wenu.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Memezelani ukuzila okungcwele; bizani ibandla elingcwele. Memani abadala labo bonke abahlala elizweni, baye endlini kaThixo uNkulunkulu wenu, likhale kuThixo.
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Maye ngalolosuku! Ngoba usuku lukaThixo seluseduze; luzafika njengencithakalo evela kuSomandla.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Ukudla akuzange kuphele phambi kwamehlo ethu, lokuthokoza kanye lokuthaba endlini kaNkulunkulu wethu na?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
Inhlanyelo itshwabhene ngaphansi kwamagade. Izindlu zamabele zingamanxiwa, iziphala zidiliziwe, ngoba amabele kawasekho.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
Yeka ukukhala kwezinkomo! Imihlambi yenkomo iyaphithizela ngoba kayilamadlelo; lemihlambi yezimvu iyahlupheka.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
Ngiyakhala kuwe Thixo, ngoba umlilo usuqede amadlelo lamalangabi asetshise zonke izihlahla zeganga.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
Lezinyamazana zeganga zifuna wena; izifula zamanzi sezicitshile njalo lomlilo usuqede amadlelo.

< Yoweli 1 >