< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
The word of the LORD that came to Joel the son of Pethuel.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hear this, ye old men, and give ear, all ye inhabitants of the land. Hath this been in your days, or in the days of your fathers?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Tell ye your children of it, and [let] your children [tell] their children, and their children another generation.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
That which the palmerworm hath left hath the locust eaten; and that which the locust hath left hath the cankerworm eaten; and that which the cankerworm hath left hath the caterpiller eaten.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Awake, ye drunkards, and weep; and howl, all ye drinkers of wine, because of the sweet wine; for it is cut off from your mouth.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For a nation is come up upon my land, strong, and without number; his teeth are the teeth of a lion, and he hath the jaw teeth of a great lion.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
He hath laid my vine waste, and barked my fig tree: he hath made it clean bare, and cast it away; the branches thereof are made white.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Lament like a virgin girded with sackcloth for the husband of her youth.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
The meal offering and the drink offering is cut off from the house of the LORD; the priests, the LORD’S ministers, mourn.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
The field is wasted, the land mourneth; for the corn is wasted, the new wine is dried up, the oil languisheth.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Be ashamed, O ye husbandmen, howl, O ye vinedressers, for the wheat and for the barley; for the harvest of the field is perished.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vine is withered, and the fig tree languisheth; the pomegranate tree, the palm tree also, and the apple tree, even all the trees of the field are withered: for joy is withered away from the sons of men.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Gird yourselves [with sackcloth], and lament, ye priests; howl, ye ministers of the altar; come, lie all night in sackcloth, ye ministers of my God: for the meal offering and the drink offering is withholden from the house of your God.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Sanctify a fast, call a solemn assembly, gather the old men [and] all the inhabitants of the land unto the house of the LORD your God, and cry unto the LORD.
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Alas for the day! for the day of the LORD is at hand, and as destruction from the Almighty shall it come,
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Is not the meat cut off before our eyes, [yea], joy and gladness from the house of our God?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
The seeds rot under their clods; the garners are laid desolate, the barns are broken down; for the corn is withered.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
How do the beasts groan! the herds of cattle are perplexed, because they have no pasture; yea, the flocks of sheep are made desolate.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
O LORD, to thee do I cry: for the fire hath devoured the pastures of the wilderness, and the flame hath burned all the trees of the field.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
Yea, the beasts of the field pant unto thee: for the water brooks are dried up, and the fire hath devoured the pastures of the wilderness.

< Yoweli 1 >