< Yobu 1 >

1 Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
Bil je mož v deželi Uc, katerega ime je bilo Job, in ta mož je bil popoln in iskren in nekdo, ki se je bal Boga in se ogibal zla.
2 Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
Tam se mu je rodilo sedem sinov in tri hčere.
3 ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
Njegovo imetje je bilo tudi sedem tisoč ovc, tri tisoč kamel, petsto jarmov volov, petsto oslic in zelo velika družina, tako da je bil ta človek največji izmed vseh mož vzhoda.
4 Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
Njegovi sinovi so šli in praznovali v svojih hišah vsak svoj dan. Poslali so in dali poklicati svoje tri sestre, da jedo in pijejo z njimi.
5 Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
Bilo je tako, da ko so se dnevi njihovega praznovanja iztekli, je Job poslal, jih posvečeval in vstajal zgodaj zjutraj ter daroval žgalne daritve glede na število njih vseh, kajti Job je rekel: »Morda so moji sinovi grešili in v svojih srcih prekleli Boga.« Tako je Job nenehno delal.
6 Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
Bil je torej dan, ko so prišli Božji sinovi, da se pokažejo pred Gospodom in tudi Satan je prišel med njimi.
7 Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
Gospod je rekel Satanu: »Od kod prihajaš?« Nató je Satan odgovoril Gospodu in rekel: »Od potikanja sem ter tja po zemlji in od hoje gor in dol po njej.«
8 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
Gospod je rekel Satanu: »Si kaj preudaril [o] mojem služabniku Jobu, ker na zemlji ni nikogar podobnega njemu; popoln in pošten človek je, ki se boji Boga in se ogiblje zla?«
9 Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
Potem je Satan odgovoril Gospodu in rekel: »Mar se Job zastonj boji Boga?
10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
Mar nisi ti naredil ograje okoli njega, okoli njegove hiše in okoli vsega, kar ima na vsaki strani? Blagoslovil si delo njegovih rok in njegovo imetje se je povečalo v deželi.
11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Toda iztegni sedaj svojo roko in se dotakni vsega, kar ima in preklinjal te bo v tvoj obraz.«
12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
Gospod je rekel Satanu: »Glej, vse, kar ima, je v tvoji oblasti, samo nanj ne iztegni svoje roke.« Tako je Satan odšel izpred Gospodove prisotnosti.
13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
Bil je dan, ko so njegovi sinovi in njegove hčere jedli in pili vino v hiši njihovega najstarejšega brata.
14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
K Jobu je prišel poslanec in rekel: »Voli so orali in osli so se pasli poleg njih
15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
in Sabejci so padli nadnje ter jih odvlekli proč. Da, z ostrino meča so umorili služabnike in samo jaz sam sem pobegnil, da ti povem.«
16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Medtem ko je še govoril, je prišel še drugi in rekel: »Ogenj od Boga je padel z neba in sežgal ovce in služabnike, jih použil in samo jaz sam sem pobegnil, da ti povem.«
17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Medtem ko je še govoril, je prišel še drugi in rekel: »Kaldejci so postavili tri čete in vpadli na kamele in jih odvedli proč. Da, in z ostrino meča umorili služabnike in samo jaz sam sem pobegnil, da ti povem.«
18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
Medtem ko je še govoril, je prišel še drugi in rekel: »Tvoji sinovi in tvoje hčere so jedli in pili vino v hiši njihovega najstarejšega brata.
19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Glej, iz divjine je prihrumel mogočen veter in udaril štiri vogale hiše in ta je padla na mladeniče in ti so mrtvi. Samo jaz sam sem pobegnil, da ti povem.«
20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
Potem je Job vstal, raztrgal svoje ogrinjalo, obril svojo glavo, padel dol na tla in oboževal
21 nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
ter rekel: »Nag sem prišel iz maternice svoje matere in nag se bom vrnil tja. Gospod je dal in Gospod je vzel. Blagoslovljeno bodi Gospodovo ime.«
22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”
V vsem tem Job ni grešil niti ni nespametno obdolžil Boga.

< Yobu 1 >