< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Na Hiob kasaa bio sɛ:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
“Aane, menim sɛ yei yɛ nokorɛ. Na ɛbɛyɛ dɛn na ɔdasani bɛtene wɔ Onyankopɔn anim?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Sɛ obi pɛ sɛ ɔne Onyankopɔn yiyi a, ɔrentumi nyi nsɛm apem mu baako mpo ano.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Ne nyansa mu dɔ, na ne tumi so. Hwan na ɔne no adi asie na ne ho baabiara anti?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Ɔtutu mmepɔ a wɔnnim ho hwee ɔbubu wɔn fa so wɔ nʼabufuo mu.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Ɔwoso asase firi ne siberɛ, na ɔma ne nnyinasoɔ woso biribiri.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Ɔkasa kyerɛ owia na ɛnhyerɛn, na ɔsɔ nsoromma hyerɛn ano.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Ɔno nko ara na ɔtrɛ ɔsoro mu, na ɔnante ɛpo asorɔkye so.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Ɔno ne Nwenwenente, Akokɔbaatan ne ne mma Yɛfoɔ; Nsorommabafan ne ewiem anafoɔ fam nsorommakuo no.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Ɔyɛ anwanwadeɛ a wɔntumi nte aseɛ, nsɛnkyerɛnneɛ a wɔntumi nkan.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Sɛ ɔnam me ho a, menhunu no; sɛ ɔsene a, menhunu no.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Sɛ ɔhwim kɔ a, hwan na ɔsi no kwan? Hwan na ɔbɛtumi abisa no sɛ, ‘Ɛdeɛn na woreyɛ yi?’
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Onyankopɔn nkora nʼabufuo so; Rahab aboafoɔ mpo ho popo wɔ nʼanim.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
“Na me ne hwan a me ne no bɛyiyi? Mɛyɛ dɛn anya nsɛm a me ne no de bɛgye akyinnyeɛ?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Sɛ menim mpo a, merentumi nyi nʼano; ɛno ara ne sɛ mɛsrɛ ahummɔborɔ afiri me ɔtemmufoɔ nkyɛn.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Mpo, sɛ mefrɛ no na ɔba a, mennye nni sɛ ɔbɛtie mʼasɛm.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Ɔde asorɔkye bɛdwerɛ me ama mʼapirakuro adɔɔso kwa.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Ɔremma menya mʼahome, bio. Ɔde awerɛhoɔ bɛhyɛ me ma tɔ.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Sɛ ɛba no ahoɔden a, ɔyɛ ɔhoɔdenfoɔ! Na sɛ ɛba atɛntenenee nso a, hwan na ɔbɛsamane no?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Sɛ medi bem mpo a, mʼano bɛbu me kumfɔ; sɛ me ho nni asɛm a, ɛbɛbu me fɔ.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
“Ɛwom sɛ medi bem deɛ, nanso memmu me ho; abrabɔ afono me.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Ne nyinaa yɛ pɛ; ɛno enti na meka sɛ, ‘Ɔsɛe deɛ ne ho nni asɛm ne omumuyɛfoɔ.’
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Ɛberɛ a amanehunu de owuo aba no, ɔsere deɛ ne ho nni asɛm no akomatuo.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Ɛberɛ a asase akɔ amumuyɛfoɔ nsam no, ɔfira ɛso atemmufoɔ ani. Sɛ ɛnyɛ ɔno a, na ɛyɛ hwan?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
“Me nna ho yɛ herɛ sene ommirikatufoɔ; ɛsene kɔ a anigyeɛ kakra mpo nni mu.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Ɛtwam kɔ sɛ akodoɔ a wɔde paparɔs ayɛ te sɛ akɔdeɛ a wɔreto akyere wɔn ahaboa.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Sɛ meka sɛ, ‘Me werɛ mfiri mʼanwiinwii, mɛsesa me nsɛm ka, na masere a,’
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
me yea ahodoɔ no bɔ me hu ara. Na menim sɛ, woremmu me bem.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Woabu me fɔ dada enti, adɛn na ɛsɛ sɛ meha me ho kwa?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Mpo sɛ ɛba sɛ mede samina dware na mede samina hohoro me nsa ho a,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
wobɛto me atwene atɛkyɛ amena mu, ama mʼatadeɛ mpo akyiri me.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
“Ɔnyɛ onipa te sɛ me na mayi nʼano, na yɛakɔgyina asɛnniiɛ abobɔ yɛn nkuro.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Sɛ anka obi wɔ hɔ a ɔbɛsiesie yɛn ntam na waka yɛn baanu abɔ mu a,
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
obi a ɔbɛyi Onyankopɔn abaa afiri me so, sɛdeɛ nʼahunahuna mmɔ me hu bio a,
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
anka mɛkasa a merensuro no, nanso saa tebea a mewɔ mu yi deɛ, mentumi.

< Yobu 9 >