< Yobu 9 >
1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Y respondió Job, y dijo:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Ciertamente yo conozco que es así; ¿y cómo se justificará el hombre con Dios?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Si quisiere contender con él, no le podrá responder a una cosa de mil.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
El es sabio de corazón, y fuerte en fuerza, ¿quién se endureció contra él, y quedó en paz?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Que arranca los montes con su furor, y no conocen quién los trastornó;
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
que remueve la tierra de su lugar, y hace temblar sus columnas;
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
que manda al sol, y no sale; y sella las estrellas.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
El solo extiende los cielos, y anda sobre las alturas del mar.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
El que hizo la Osa, y el Orión, y las Pléyades, y los lugares secretos del mediodía;
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
el que hace cosas grandes e incomprensibles, y maravillosas, sin número.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
He aquí que él pasará delante de mí, y yo no lo veré; y pasará, y no lo entenderé.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
He aquí, arrebatará; ¿quién le hará restituir? ¿Quién le dirá: Qué haces?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Dios no tornará atrás su ira, y debajo de él se encorvan los que ayudan a la soberbia.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
¿Cuánto menos le responderé yo, y eligiré mis palabras con él?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Que aunque yo sea justo, no responderé; antes habré de rogar a mi juez.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Que si yo le invocase, y él me respondiese, aún no creeré que haya escuchado mi voz.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Porque me ha quebrado con tempestad, y ha aumentado mis heridas sin causa.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Que aún no me ha concedido que tome mi aliento; mas me ha llenado de amarguras.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Si habláramos de su potencia, fuerte por cierto es; si de su juicio, ¿quién me emplazará?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Si yo me justificare, me condenará mi boca; si me predicare perfecto, él me hará inicuo.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Si yo me predicare imperfecto, no conozco mi alma; condenaré mi vida.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Una cosa resta es a saber que yo diga: Al perfecto y al impío él los consume.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Si es azote, mate de presto, y no se ría de la prueba de los inocentes.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
La tierra es entregada en manos de los impíos, y él cubre el rostro de sus jueces. Si no es él el que lo hace, ¿quién es? ¿Dónde está?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Mis días han sido más ligeros que un correo; huyeron, y nunca vieron bien.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Pasaron con los navíos de Ebeh; o como el águila que se arroja a la presa.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Si digo: Quiero olvidar mi queja, dejaré mi aburrimiento, y me esforzaré.
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
Temo todos mis trabajos; sé que no me perdonarás.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Si yo soy impío, ¿para qué trabajaré en vano?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Aunque me lave con aguas de nieve, y aunque limpie mis manos con la misma limpieza,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
aún me hundirás en el hoyo; y mis propios vestidos me abominarán.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Porque no es hombre como yo, para que yo le responda, y vengamos juntamente a juicio.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
No hay entre nosotros árbitro que ponga su mano sobre nosotros ambos.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Quite de sobre mí su verdugo, y su terror no me perturbe.
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Y hablaré, y no le temeré; porque en este estado no estoy en mí.