< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
А Јов одговори и рече:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Заиста, знам да је тако; јер како би могао човек бити прав пред Богом?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Ако би се хтео прети с Њим, не би Му могао одговорити од хиљаде на једну.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Мудар је срцем и јак снагом; ко се је опро Њему и био срећан?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Он премешта горе, да нико и не опази; превраћа их у гневу свом;
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Он креће земљу с места њеног да јој се ступови дрмају;
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Он кад запрети сунцу, не излази; Он запечаћава звезде;
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Он разапиње небо сам, и гази по валима морским;
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Он је начинио звезде кола и штапе и влашиће и друге југу у дну;
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Он чини ствари велике и неиспитиве и дивне, којима нема броја.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Гле, иде мимо мене, а ја не видим; прође, а ја га не опазим.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Гле, кад ухвати, ко ће Га нагнати да врати? Ко ће Му казати: Шта радиш?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Бог не устеже гнева свог, падају пода Њ охоли помоћници.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
А како би Му ја одговарао и бирао речи против Њега?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Да сам и прав, нећу Му се одговорити, ваља да се молим судији свом.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Да Га зовем и да ми се одзове, још не могу веровати да је чуо глас мој.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Јер ме је вихором сатро и задао ми много рана низашта.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Не да ми да одахнем, него ме сити горчинама.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Ако је на силу, гле, Он је најсилнији; ако на суд, ко ће ми сведочити?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Да се правдам, моја ће ме уста осудити; да сам добар, показаће да сам неваљао.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Ако сам добар, нећу знати за то; омрзао ми је живот мој.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Свеједно је; зато рекох: и доброг и безбожног Он потире.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Кад би још убио бич наједанпут! Али се смеје искушавању правих.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Земља се даје у руке безбожнику; лице судија њених заклања; ако не Он, да ко?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Али дани моји бише бржи од гласника; побегоше, не видеше добра.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Прођоше као брзе лађе, као орао кад лети за храну.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Ако кажем: Заборавићу тужњаву своју, оставићу гнев свој и окрепићу се;
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
Страх ме је од свих мука мојих, знам да ме нећеш оправдати.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Бићу крив; зашто бих се мучио узалуд?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Да се измијем водом снежницом, и да очистим сапуном руке своје,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
Тада ћеш ме замочити у јаму да се гаде на ме моје хаљине.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Јер није човек као ја да Му одговарам, да идем с Њим на суд;
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Нити има међу нама кмета да би ставио руку своју међу нас двојицу.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Нека одмакне од мене прут свој, и страх Његов нека ме не страши;
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Тада ћу говорити, и нећу Га се бојати; јер овако не знам за себе.

< Yobu 9 >