< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Йов а луат кувынтул ши а зис:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
„Штиу бине кэ есте аша. Ши кум ар путя омул сэ-шь скоатэ дрептате ынаинтя луй Думнезеу?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Дакэ ар вои сэ се черте ку Ел, дин о мие де лукрурь н-ар путя сэ рэспундэ ла унул сингур.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Але Луй сунт ынцелепчуня ши атотпутерничия: чине И с-ар путя ымпотриви фэрэ сэ фие педепсит?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Ел мутэ деодатэ мунций ши-й рэстоарнэ ын мыния Са.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Згудуе пэмынтул дин темелия луй, де и се клатинэ стылпий.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Порунчеште соарелуй, ши соареле ну май рэсаре; ши цине стелеле суб печетя Луй.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Нумай Ел ынтинде черуриле ши умблэ пе ынэлцимиле мэрий.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Ел а фэкут Урса-Маре, Лучяфэрул де сярэ ши Ралицеле ши стелеле дин цинутуриле де мязэзи.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Ел фаче лукрурь марь ши непэтрунсе, минунь фэрэ нумэр.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Ятэ, Ел трече пе лынгэ мине, ши ну-Л вэд, Се дуче, ши ну-Л зэреск.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Дакэ апукэ Ел, чине-Л ва опри? Чине-Й ва зиче: ‘Че фачь?’
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Думнезеу ну-Шь ынтоарче мыния; суб Ел се плякэ тоць сприжиниторий мындрией.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Ши еу кум сэ-Й рэспунд? Че кувинте сэ алег?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Кяр дакэ аш авя дрептате, ну Й-аш рэспунде. Ну пот декыт сэ мэ рог жудекэторулуй.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Ши кяр дакэ м-ар аскулта кынд Ыл кем, тот н-аш путя креде кэ мь-а аскултат гласул –
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Ел, каре мэ избеште ка ынтр-о фуртунэ, каре ымь ынмулцеште фэрэ причинэ рэниле,
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
каре ну мэ ласэ сэ рэсуфлу, мэ сатурэ де амэрэчуне.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Сэ алерг ла путере? Ел есте атотпутерник. Ла дрептате? Чине мэ ва апэра?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Орькытэ дрептате аш авя, гура мя мэ ва осынди ши орькыт де невиноват аш фи, Ел мэ ва арэта ка виноват.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Невиноват! Сунт, дар ну цин ла вяцэ, ымь диспрецуеск вяца.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Че-мь пасэ ла урма урмей? Кэч ындрэзнеск с-о спун: Ел нимичеште пе чел невиноват ка ши пе чел виноват.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Ши дакэ бичул ар причинуи мэкар ындатэ моартя…! Дар Ел рыде де ынчеркэриле челуй невиноват.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Пэмынтул есте дат пе мыниле челуй нелеӂюит; Ел акоперэ окий жудекэторилор – де ну Ел, апой чине алтул?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Зилеле меле аляргэ май юць декыт ун алергэтор; фуг фэрэ сэ фи вэзут феричиря;
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
трек ка ши корэбииле челе юць, ка вултурул каре се репеде асупра прэзий.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Дакэ зик: ‘Вряу сэ-мь уйт суферинцеле, сэ-мь лас ынтристаря ши сэ фиу войос’,
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
сунт ынгрозит де тоате дурериле меле. Штиу кэ ну мэ вей скоате невиноват.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Ши дакэ вой фи жудекат виноват, пентру че сэ мэ май трудеск деӂяба?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Кяр дакэ м-аш спэла ку зэпадэ, кяр дакэ мь-аш курэци мыниле ку лешие,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
Ту тот м-ай куфунда ын мочирлэ, де с-ар скырби пынэ ши хайнеле де мине!
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Кэч Ел ну есте ун ом ка мине, ка сэ-Й пот рэспунде ши сэ мерӂем ымпреунэ ла жудекатэ.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Нич ну есте вреун мижлочитор ынтре ной, каре сэ-шь пунэ мына песте ной амындой.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Сэ-Шь трагэ ынсэ варга де дясупра мя ши сэ ну мэ май тулбуре спайма Луй.
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Атунч вой ворби ши ну мэ вой теме де Ел. Алтфел, ну сунт стэпын пе мине.

< Yobu 9 >