< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
A Hiob odpowiedział:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Doprawdy, wiem, że tak [jest]. Lecz jak człowiek miałby być usprawiedliwiony przed Bogiem?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Gdyby chciał się z nim spierać, nie odpowie mu ani raz na tysiąc.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Ma on mądre serce i potężną siłę. Kto mu się sprzeciwił i powodziło mu się?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
On przenosi góry, a [ludzie] nie zauważają, przewraca je w swoim gniewie.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
On wstrząsa ziemią z jej miejsca i trzęsą się jej filary.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
On rozkaże słońcu i ono nie wschodzi, zamyka też gwiazdy pieczęcią.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
On sam rozciąga niebiosa i kroczy po falach morza.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
On stworzył Niedźwiedzicę, Oriona, Plejady i gwiazdozbiory południa.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
On czyni rzeczy wielkie i niezbadane, cuda, których zliczyć nie można.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Oto przechodzi obok mnie, a nie widzę go; mija mnie, a ja go nie dostrzegam.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Oto gdy zabiera, któż go powstrzyma? Któż mu powie: Co czynisz?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Gdyby Bóg nie odwrócił swego gniewu, zuchwali pomocnicy upadliby pod nim.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Jakże ja mu odpowiem? [Jakie] słowa wybiorę, aby się z nim spierać?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Choćbym był sprawiedliwy, nie odpowiedziałbym mu, lecz błagałbym swojego sędziego.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Choćbym go wzywał, a on by się odezwał, jeszcze nie uwierzyłbym, że mnie wysłuchał;
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Kruszy mnie bowiem burzą i pomnaża moje rany bez powodu.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Nie pozwala mi odetchnąć, raczej napełnia mnie goryczą.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Jeśli [chodzi] o siłę, oto jest potężny, a jeśli chodzi o sąd, któż mnie przed nim przyprowadzi?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Jeśli się usprawiedliwię, moje usta mnie potępią. Jeśli powiem, że jestem doskonały, to one wykażą, że jestem przewrotny.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Choćbym był doskonały, przecież nie znałbym swojej duszy; gardziłbym swoim życiem.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Jedno jest [pewne], dlatego powiedziałem: On niszczy [zarówno] doskonałego, [jak] i niegodziwego;
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Jeśli bicz nagle zabija, śmieje się on z doświadczenia niewinnych.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Ziemia została wydana w ręce niegodziwego. On zakrywa oblicze sędziów. A jeśli nie on, któż [to czyni]?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Ale moje dni są szybsze niż goniec, uciekły i nie widziały nic dobrego.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Przeminęły jak szybkie łodzie, jak orzeł, który rzuca się na żer.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Jeśli powiem: Zapomnę o swojej skardze, zaniecham swego gniewu i pocieszę się;
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
Wtedy przerażają mnie wszystkie moje cierpienia, bo wiem, że nie uznasz mnie za niewinnego.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Jeśli jestem niegodziwy, to czemu trudzę się na próżno?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Choćbym się umył wodą ze śniegu i oczyścił mydłem swoje ręce;
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
Ty i tak zanurzysz mnie w dole i moje szaty będą się mną brzydzić.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
On bowiem nie jest człowiekiem jak ja, abym śmiał mu odpowiedzieć i abyśmy razem stanęli przed sądem.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Nie ma między nami rozjemcy, który mógłby położyć rękę na nas obu.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Niech tylko zdejmie ze mnie swoją rózgę, a jego groza niech mnie już nie przeraża;
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Wtedy będę mówił i nie będę się go bać; ale tak nie jest ze mną.

< Yobu 9 >