< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Da tok Job til orde og sa:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Ja visst, jeg vet at det er så; hvorledes skulde en mann kunne ha rett mot Gud?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Om han hadde lyst til å gå i rette med Gud, kunde han ikke svare ham ett til tusen.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Vis som han er av hjerte og veldig i styrke - hvem trosset ham og kom vel fra det,
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
han som flytter fjell før de vet av det, som velter dem i sin vrede,
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
som ryster jorden, så den viker fra sitt sted, og dens støtter bever,
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
som byder solen, så den ikke går op, og som setter segl for stjernene,
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
som alene utspenner himmelen og skrider frem over havets høider,
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
som har skapt Bjørnen, Orion og Syvstjernen og Sydens stjernekammere,
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
som gjør store, uransakelige ting og under uten tall?
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Han går forbi mig, og jeg ser ham ikke; han farer forbi, og jeg merker ham ikke.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Han griper sitt rov - hvem vil hindre ham, hvem vil si til ham: Hvad gjør du?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Gud holder ikke sin vrede tilbake; under ham måtte Rahabs hjelpere bøie sig.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Hvorledes skulde da jeg kunne svare ham og velge mine ord imot ham,
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
jeg som ikke kunde svare om jeg enn hadde rett, men måtte be min dommer om nåde!
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Om jeg ropte, og han svarte mig, kunde jeg ikke tro at han hørte min røst,
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
han som vilde knuse mig i storm og uten årsak ramme mig med sår på sår,
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
som ikke vilde tillate mig å dra ånde, men vilde mette mig med lidelser.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Gjelder det styrke, så sier han: Se, her er jeg! Gjelder det rett: Hvem vil stevne mig?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Hadde jeg enn rett, skulde dog min egen munn dømme mig skyldig; var jeg enn uskyldig, vilde han dog si at jeg hadde urett.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Skyldløs er jeg; jeg bryr mig ikke om å leve - jeg forakter mitt liv.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Det kommer ut på ett; derfor sier jeg: Skyldløs eller ugudelig - han gjør dem begge til intet.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Når svepen brått rammer med død, spotter han de uskyldiges lidelse.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Jorden er gitt i den ugudeliges hånd; han tilhyller dens dommeres åsyn. Er det ikke han som gjør det, hvem er det da?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Mine dager har vært hastigere enn en løper; de er bortflyktet uten å ha sett noget godt;
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
de har faret avsted som båter av rør, som en ørn som slår ned på sitt bytte.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Om jeg sier: Jeg vil glemme min sorg, jeg vil la min mørke mine fare og se glad ut,
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
da gruer jeg for alle mine plager; jeg vet jo at du ikke frikjenner mig.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Jeg skal jo være ugudelig - hvorfor gjør jeg mig da forgjeves møie?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Om jeg tvettet mig med sne og renset mine hender med lut,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
da skulde du dyppe mig i en grøft, så mine klær vemmedes ved mig.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
For han er ikke en mann som jeg, så jeg kunde svare ham, så vi kunde gå sammen for retten;
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
det er ikke nogen voldgiftsmann mellem oss, som kunde legge sin hånd på oss begge.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Når han bare tok sitt ris bort fra mig, og hans redsler ikke skremte mig!
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Da skulde jeg tale uten å reddes for ham; for slik er jeg ikke, det vet jeg med mig selv.

< Yobu 9 >