< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Alors Job répondit,
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
« Je sais en vérité qu'il en est ainsi, mais comment l'homme peut-il être juste avec Dieu?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
S'il lui plaît de contester avec lui, il ne peut pas lui répondre une fois sur mille.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Dieu est sage de cœur et puissant de force. Qui s'est endurci contre lui et a prospéré?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Il enlève les montagnes, et ils ne le savent pas, quand il les renverse dans sa colère.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Il secoue la terre de sa place. Ses piliers tremblent.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Il commande au soleil et il ne se lève pas, et scelle les étoiles.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Lui seul étend les cieux, et marche sur les vagues de la mer.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Il crée l'Ours, Orion et les Pléiades, et les chambres du sud.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Il fait de grandes choses qu'on ne peut pas savoir; oui, des choses merveilleuses sans nombre.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Voici qu'il passe à côté de moi, et je ne le vois pas. Il passe aussi, mais je ne le perçois pas.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Voici qu'il arrache. Qui peut l'en empêcher? Qui lui demandera: « Que fais-tu?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
« Dieu ne retire pas sa colère. Les aides de Rahab s'abaissent sous lui.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
A plus forte raison lui répondrai-je, et choisir mes mots pour argumenter avec lui?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Même si j'étais juste, je n'ai pas voulu lui répondre. Je ferais des supplications à mon juge.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Si j'avais appelé, et qu'il m'ait répondu, pourtant je ne croirais pas qu'il ait écouté ma voix.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Car il me brise par une tempête, et multiplie mes blessures sans raison.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Il ne me permettra pas de reprendre mon souffle, mais me remplit d'amertume.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Si c'est une question de force, voici qu'il est puissant! S'il s'agit de justice, « Qui, dit-il, me convoquera?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Bien que je sois juste, ma propre bouche me condamne. Bien que je sois irréprochable, cela prouvera ma perversité.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Je suis irréprochable. Je ne me respecte pas. Je méprise ma vie.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
« C'est la même chose. C'est pourquoi je dis qu'il détruit les irréprochables et les méchants.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Si le fléau tue soudainement, il se moquera du procès des innocents.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
La terre est livrée entre les mains des méchants. Il couvre les visages de ses juges. Si ce n'est pas lui, alors qui est-ce?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
« Maintenant mes jours sont plus rapides qu'un coureur. Ils s'enfuient. Ils ne voient pas le bien.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Ils ont disparu comme les navires rapides, comme l'aigle qui se jette sur sa proie.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Si je dis: « J'oublierai ma plainte », J'enlèverai mon visage triste, et je me réjouirai,
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
J'ai peur de tous mes chagrins. Je sais que vous ne me tiendrez pas pour innocent.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Je serai condamné. Alors pourquoi je travaille en vain?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Si je me lave avec de la neige, et je nettoie mes mains avec de la soude,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
pourtant tu me plongeras dans le fossé. Mes propres vêtements me feront horreur.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Car il n'est pas un homme, comme moi, pour que je lui réponde, que nous devrions nous réunir pour juger.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Il n'y a pas d'arbitre entre nous, qui pourrait poser sa main sur nous deux.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Qu'il éloigne de moi son bâton. Que sa terreur ne me fasse pas peur;
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
alors je parlerais, et je ne le craindrais pas, car je ne le suis pas en moi-même.

< Yobu 9 >