< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered and said,
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
I know [it to be] so of a truth: but how should man be just with God?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
If he will contend with him, he cannot answer him one of a thousand.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
[He is] wise in heart, and mighty in strength: who hath hardened [himself] against him, and hath prospered?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Who removeth the mountains, and they know not: who overturneth them in his anger.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Who shaketh the earth out of her place, and its pillars tremble.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Who commandeth the sun, and it riseth not; and sealeth up the stars.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Who alone spreadeth out the heavens, and treadeth upon the waves of the sea.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Who maketh Arcturus, Orion, and Pleiades, and the chambers of the south.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Who doeth great things past finding out; yes, and wonders without number.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Lo, he goeth by me, and I see [him] not: he passeth on also, but I perceive him not.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Behold, he taketh away, who can hinder him? who will say to him, What doest thou?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
[If] God will not withdraw his anger, the proud helpers do stoop under him.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
How much less shall I answer him, [and] choose out my words [to reason] with him?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Whom, though I were righteous, [yet] would I not answer, [but] I would make supplication to my judge.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
If I had called, and he had answered me; [yet] I would not believe that he had hearkened to my voice.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
For he breaketh me with a tempest, and multiplieth my wounds without cause.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
He will not suffer me to take my breath, but filleth me with bitterness.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
If [I speak] of strength, lo, [he is] strong: and if of judgment, who shall set me a time [to plead]?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
If I justify myself, my own mouth will condemn me: [if I say], I [am] perfect, that also will prove me perverse.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
[Though] I [were] perfect, [yet] would I not know my soul: I would despise my life.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
This [is] one [thing], therefore I said [it], he destroyeth the perfect and the wicked.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
If the scourge shall slay suddenly, he will laugh at the trial of the innocent.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
The earth is given into the hand of the wicked: he covereth the faces of its judges; if not, where, [and] who [is] he?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Now my days are swifter than a post: they flee away, they see no good.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
They are passed away as the swift ships: as the eagle [that] hasteth to the prey.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
If I say, I will forget my complaint, I will leave off my heaviness, and comfort [myself]:
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
I am afraid of all my sorrows, I know that thou wilt not hold me innocent.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
[If] I am wicked, why then do I labor in vain?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
If I wash myself with snow water, and make my hands never so clean;
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
Yet wilt thou plunge me in the ditch, and my own clothes shall abhor me.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
For [he is] not a man, as I [am], [that] I should answer him, [and] we should come together in judgment.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Neither is there any judge between us, [that] might lay his hand upon us both.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Let him take away his rod from me, and let not his fear terrify me:
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
[Then] would I speak, and not fear him; but [it is] not so with me.

< Yobu 9 >