< Yobu 9 >
1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered and said:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
Of a truth, I know that it is so: For how can man be just before God?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
If he choose to contend with him, He cannot answer him to one charge of a thousand.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
He is excellent in wisdom, mighty in strength: Who hath hardened himself against him, and prospered?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
He removeth the mountains, and they know it not; He overturneth them in his anger.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
He shaketh the earth out of her place, And the pillars thereof tremble.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
He commandeth the sun, and it riseth not, And he sealeth up the stars.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
He alone spreadeth out the heavens, And walketh upon the high waves of the sea.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
He made the Bear, Orion, and the Pleiades, And the secret chambers of the South.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
He doeth great things past finding out, Yea, wonderful things without number.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Lo! he goeth by me, but I see him not; He passeth along, but I do not perceive him.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Lo! he seizeth, and who can hinder him? Who will say to him, What doest thou?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
God will not turn away his anger; The proud helpers are brought low before him.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
How much less shall I answer him, And choose out words to contend with him?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Though I were innocent, I would not answer him; I would cast myself on the mercy of my judge.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Should I call, and he make answer to me, I could not believe that he listened to my voice, —
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
He who falleth upon me with a tempest, And multiplieth my wounds without cause!
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Who will not suffer me to take my breath, But filleth me with bitterness!
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
If I look to strength, “Lo! here am I!” [[saith he, ]] If to justice, “Who shall summon me to trial?”
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Though I were upright, yet must my own mouth condemn me; Though I were innocent, He would prove me perverse.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Though I were innocent, I would not care for myself; I would despise my life.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
It is all one; therefore I will affirm, He destroyeth the righteous and the wicked alike.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
When the scourge bringeth sudden destruction, He laugheth at the sufferings of the innocent.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
The earth is given into the hands of the wicked; He covereth the face of the judges thereof; If it be not He, who is it?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
My days have been swifter than a courier; They have fled away; they have seen no good.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
They have gone by like the reed-skiffs; Like the eagle, darting upon his prey.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
If I say, I will forget my lamentation, I will change my countenance, and take courage,
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
Still am I in dread of the multitude of my sorrows; For I know that thou wilt not hold me innocent.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
I shall be found guilty; Why then should I labor in vain?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
If I wash myself in snow, And cleanse my hands with lye,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
Still wilt thou plunge me into the pit, So that my own clothes will abhor me.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
For He is not a man, as I am, that I may contend with him, And that we may go together into judgment;
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
There is no umpire between us, Who may lay his hand upon us both.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Let him take from me his rod, And not dismay me with his terrors,
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Then I will speak, and not be afraid of him: For I am not so at heart.