< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Så tog Job til Orde og svarede:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
"Jeg ved forvist, at således er det, hvad Ret har en dødelig over for Gud?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Vilde Gud gå i Rette med ham, kan han ikke svare på et af tusind!
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Viis af Hjerte og vældig i Kraft hvo trodsede ham og slap vel derfra?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Han flytter Bjerge så let som intet, vælter dem om i sin Vrede,
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
ryster Jorden ud af dens Fuger, så dens Grundstøtter bæver;
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
han taler til solen, så skinner den ikke, for Stjernerne sætter han Segl,
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
han udspænder Himlen ene, skrider hen over Havets Kamme,
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
han skabte Bjørnen, Orion, Syvstjernen og Sydens Kamre,
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
han øver ufattelig Vælde og Undere uden Tal!
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Går han forbi mig, ser jeg ham ikke, farer han hen, jeg mærker ham ikke;
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
røver han, hvem mon der hindrer ham i det? Hvo siger til ham: "Hvad gør du?"
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Gud lægger ikke Bånd på sin Vrede, Rahabs Hjælpere bøjed sig under ham;
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
hvor kan jeg da give ham Svar og rettelig føje min Tale for ham!
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Har jeg end Ret, jeg kan dog ej svare, må bede min Dommer om Nåde!
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
Nævned jeg ham, han svared mig ikke, han hørte, tror jeg, ikke min Røst,
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
han, som river mig bort i Stormen, giver mig - Sår på Sår uden Grund,
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
ikke lader mig drage Ånde, men lader mig mættes med beskeing.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Gælder det Kæmpekraft, melder han sig! Gælder det Ret, hvo stævner ham da!
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Har jeg end Ret, må min Mund dog fælde mig, er jeg end skyldfri, han gør mig dog vrang!
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Skyldfri er jeg, ser bort fra min Sjæl og agter mit Liv for intet!
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Lige meget; jeg påstår derfor: Skyldfri og skyldig gør han til intet!
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
Når Svøben kommer med Død i et Nu, så spotter han skyldfries Hjertekval;
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
Jorden gav han i gudløses Hånd, hylder dens Dommeres Øjne til, hvem ellers, om ikke han?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Raskere end Løberen fløj mine Dage, de svandt og så ikke Lykke,
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
gled hen som Både af Si, som en Ørn, der slår ned på Bytte.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Dersom jeg siger: "Mit Suk vil jeg glemme, glatte mit Ansigt og være glad,"
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
må jeg dog grue for al min Smerte, jeg ved, du kender mig ikke fri.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Jeg skal nu engang være skyldig, hvorfor da slide til ingen Nytte?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Toed jeg mig i Sne og tvætted i Lud mine Hænder,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
du dypped mig dog i Pølen, så Klæderne væmmedes ved mig.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Thi du er ikke en Mand som jeg, så jeg kunde svare, så vi kunde gå for Retten sammen;
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
vi savner en Voldgiftsmand til at lægge sin Hånd på os begge!
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Fried han mig for sin Stok, og skræmmed hans Rædsler mig ikke,
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
da talte jeg uden at frygte ham, thi min Dom om mig selv er en anden!

< Yobu 9 >