< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Job progovori i reče:
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
“Zaista, dobro ja znadem da je tako: kako da pred Bogom čovjek ima pravo?
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
Ako bi se tkogod htio prÓeti s njime, odvratio mu ne bi ni jednom od tisuću.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
Srcem on je mudar, a snagom svesilan, i tko bi se njemu nekažnjeno opro?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
On brda premješta, a ona to ne znaju, u jarosti svojoj on ih preokreće.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Pokreće on zemlju sa njezina mjesta, iz temelja njene potresa stupove.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Kad zaprijeti suncu, ono se ne rađa, on pečatom svojim i zvijezde pečati.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Jedini on je nebesa razapeo i pučinom morskom samo on hodao.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Stvorio je Medvjede i Oriona, Vlašiće i zvijezđa na južnome nebu.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Tvorac on je djela silnih, nepojmljivih čudesa koja se izbrojit' ne mogu.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
Ide pored mene, a ja ga ne vidim; evo, on prolazi - ja ga ne opažam.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
Ugrabi li što, tko će mu to priječit, i tko ga pitat smije: 'Što si učinio?'
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
Bog silni srdžbu svoju ne opoziva: pred njim poniču saveznici Rahaba.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Pa kako onda da njemu odgovorim, koju riječ da protiv njega izaberem?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
I da sam u pravu, odvratio ne bih, u suca svojega milost bih molio.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
A kad bi se na zov moj i odazvao, vjerovao ne bih da on glas moj sluša.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
Jer, za dlaku jednu on mene satire, bez razloga moje rane umnožava.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
Ni časa jednoga predahnut' mi ne da, nego mene svakom gorčinom napaja!
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
Ako je na snagu - tÓa on je najjači! Ako je na pravdu - tko će njega na sud?
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
Da sam i prav, usta bi me osudila, da sam i nevin, zlim bi me proglasila.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
A jesam li nevin? Ni sam ne znam više, moj je život meni sasvim omrzao!
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
Jer, to je svejedno; i zato ja kažem: nevina i grešnika on dokončava.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
I bič smrtni kad bi odjednom ubijo ... ali on se ruga nevolji nevinih.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
U zemlji predanoj u šake zlikovaca, on oči sucima njezinim zastire. Ako on to nije, tko je drugi onda?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Od skoroteče su brži moji dani, bježe daleko, nigdje dobra ne videć.'
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
K'o čamci od rogoza hitro promiču, k'o orao na plijen kada se zaleti.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Kažem li: zaboravit ću jadikovku, razvedrit ću lice i veseo biti,
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
od mojih me muka groza obuzima, jer znadem da me ti ne držiš nevinim.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Ako li sam grešan, tÓa čemu onda da zalud mučim sebe.
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Kad bih i sniježnicom sebe ja isprao, kad bih i lugom ruke svoje umio,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
u veću bi me nečist opet gurnuo, i moje bi me se gnušale haljine!
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Nije čovjek k'o ja da se s njime pravdam i na sud da idem s njim se parničiti.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
Niti kakva suca ima među nama da ruke svoje stavi na nas dvojicu,
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
da šibu njegovu od mene odmakne, da užas njegov mene više ne plaši!
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Govorit ću ipak bez ikakva straha, jer ja nisam takav u svojim očima!

< Yobu 9 >