< Yobu 8 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Kisha Bildadi Mshuhi akajibu:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
“Hata lini wewe utasema mambo kama haya? Maneno yako ni kama upepo mkuu.
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Je, Mungu hupotosha hukumu? Je, Mwenyezi hupotosha kile kilicho haki?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Watoto wako walipomtenda dhambi, aliwapa adhabu ya dhambi yao.
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
Lakini ukimtafuta Mungu, nawe ukamsihi Mwenyezi,
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
ikiwa wewe ni safi na mnyofu, hata sasa atainuka mwenyewe kwa niaba yako, na kukurudisha katika mahali pako pa haki.
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
Ijapokuwa mwanzo wako ulikuwa mdogo, lakini mwisho wako utakuwa wa mafanikio.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
“Ukaulize vizazi vilivyotangulia na uone baba zao walijifunza nini,
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
kwa kuwa sisi tumezaliwa jana tu na hatujui lolote, nazo siku zetu duniani ni kama kivuli tu.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
Je, hawatakufundisha na kukueleza? Je, hawataleta maneno kutoka kwenye kufahamu kwao?
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Je, mafunjo yaweza kumea mahali pasipo na matope? Matete yaweza kustawi bila maji?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
Wakati bado yanaendelea kukua kabla ya kukatwa, hunyauka haraka kuliko majani mengine.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Huu ndio mwisho wa watu wote wanaomsahau Mungu; vivyo hivyo matumaini ya wasiomjali Mungu huangamia.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
Lile analolitumainia huvunjika upesi; lile analolitegemea ni utando wa buibui.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
Huutegemea utando wake, lakini hausimami; huungʼangʼania, lakini haudumu.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
Yeye ni kama mti ulionyeshewa vizuri wakati wa jua, ukieneza machipukizi yake bustanini;
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
huifunganisha mizizi yake kwenye lundo la mawe, na kutafuta nafasi katikati ya mawe.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Unapongʼolewa kutoka mahali pake, ndipo mahali pale huukana na kusema, ‘Mimi kamwe sikukuona.’
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
Hakika uhai wake hunyauka, na kutoka udongoni mimea mingine huota.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
“Hakika Mungu hamkatai mtu asiye na hatia, wala kuitia nguvu mikono ya mtenda mabaya.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
Bado atakijaza kinywa chako na kicheko, na midomo yako na kelele za shangwe.
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Adui zako watavikwa aibu, nazo hema za waovu hazitakuwepo tena.”

< Yobu 8 >