< Yobu 8 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Tad Bildads no Šuhas atbildēja un sacīja:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Cik ilgi tu tā gribi runāt? tavas mutes vārdi ir kā stiprs vējš, kas greznojās.
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Vai Dievs pārgrozītu tiesu, un tas Visuvarenais pārgrozītu taisnību?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Kad tavi bērni pret Viņu grēkojuši, tad Viņš tos arī nodevis viņu grēku varā.
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
Bet ja tu pie laika to stipro Dievu meklēsi un no tā Visuvarenā žēlastības lūgsies,
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Ja tu šķīsts būsi un taisns, tad Viņš tevi gan uzlūkos un atkal uztaisīs tavas taisnības dzīvokli.
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
Un ja tu iesākumā biji sīks, pēcgalā tu būsi ļoti liels.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
Jo vaicā jel tiem senajiem, un liec vērā, ko viņu tēvi piedzīvojuši.
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
Jo mēs esam vakarēji un nezinām nenieka; jo mūsu dienas ir kā ēna virs zemes.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
Viņi tevi gan mācīs un tev sacīs un no savas sirds runās.
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Vai ašķi aug bez dūņām, vai niedres izaug bez ūdens?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
Vēl zaļo, netiek plūktas, bet nokalst ātrāki nekā visa cita zāle.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Tā iet visiem, kas Dievu aizmirst, un blēža cerība iet bojā,
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
Viņa drošums iznīkst, un viņa patvērums ir kā zirnekļa tīkls.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
Viņš atslienas pie sava nama, bet tas nestāv, viņš gan pie tā turas, bet tas nepastāv.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
Gan viņš ir zaļš, saulei spīdot, un viņa zari izplešas viņa dārzā,
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
Viņa saknes vijās ap akmeņiem un ķērās pie mūra ēkas.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Kad viņš to izdeldē no viņa vietas, tad šī viņu aizliedz: Es tevi neesmu redzējusi.
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
Redzi, tāds ir viņa ceļa prieks, un no pīšļiem izaug atkal citi.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
Redzi, Dievs neatmet sirdsskaidro, un neņem bezdievīgo pie rokas.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
Kamēr Viņš tavu muti piepildīs ar smiešanos un tavas lūpas ar gavilēšanu,
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Tavi ienaidnieki taps apģērbti ar kaunu, un bezdievīgo dzīvokļa vairs nebūs.

< Yobu 8 >