< Yobu 8 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Respondens autem Baldad Suhites, dixit:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Usquequo loqueris talia, et spiritus multiplex sermones oris tui?
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Numquid Deus supplantat iudicium? aut Omnipotens subvertit quod iustum est?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Etiam si filii tui peccaverunt ei, et dimisit eos in manu iniquitatis suae:
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
Tu tamen si diluculo consurrexeris ad Deum, et Omnipotentem fueris deprecatus:
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Si mundus et rectus incesseris, statim evigilabit ad te, et pacatum reddet habitaculum iustitiae tuae:
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
In tantum, ut si priora tua fuerint parva, et novissima tua multiplicentur nimis.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
Interroga enim generationem pristinam, et diligenter investiga patrum memoriam:
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
(Hesterni quippe sumus, et ignoramus quoniam sicut umbra dies nostri sunt super terram.)
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
Et ipsi docebunt te: loquentur tibi, et de corde suo proferent eloquia.
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Numquid vivere potest scirpus absque humore? aut crescere carectum sine aqua?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
Cum adhuc sit in flore, nec carpatur manu, ante omnes herbas arescit:
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Sic viae omnium, qui obliviscuntur Deum, et spes hypocritae peribit:
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
Non ei placebit vecordia sua, et sicut tela aranearum fiducia eius.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
Innitetur super domum suam, et non stabit: fulciet eam, et non consurget:
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
Humectus videtur antequam veniat Sol, et in ortu suo germen eius egredietur.
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
Super acervum petrarum radices eius densabuntur, et inter lapides commorabitur.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Si absorbuerit eum de loco suo, negabit eum, et dicet: Non novi te.
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
Haec est enim laetitia viae eius, ut rursum de terra alii germinentur.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
Deus non proiiciet simplicem, nec porriget manum malignis:
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
Donec impleatur risu os tuum, et labia tua iubilo.
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Qui oderunt te, induentur confusione: et tabernaculum impiorum non subsistet.

< Yobu 8 >