< Yobu 8 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Da antwortete Bildad von Suah und sprach:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Wie lange willst du solches reden und die Rede deines Mundes so einen stolzen Mut haben?
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Meinest du, daß Gott unrecht richte, oder der Allmächtige das Recht verkehre?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Haben deine Söhne vor ihm gesündiget, so hat er sie verstoßen um ihrer Missetat willen.
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
So du aber dich beizeiten zu Gott tust und dem Allmächtigen flehest,
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
und du so rein und fromm bist, so wird er aufwachen zu dir und wird wieder aufrichten die Wohnung um deiner Gerechtigkeit willen;
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
und was du zuerst wenig gehabt hast, wird hernach fast zunehmen.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
Denn frage die vorigen Geschlechter und nimm dir vor, zu forschen ihre Väter.
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
(Denn wir sind von gestern her und wissen nichts; unser Leben ist ein Schatten auf Erden.)
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
Sie werden dich's lehren und dir sagen und ihre Rede aus ihrem Herzen hervorbringen.
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Kann auch das Schilf aufwachsen, wo es nicht feucht stehet, oder Gras wachsen ohne Wasser?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
Sonst wenn's noch in der Blüte ist, ehe es abgehauen wird, verdorret es, ehe denn man Heu machet.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
So geht es allen denen, die Gottes vergessen, und die Hoffnung der Heuchler wird verloren sein.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
Denn seine Zuversicht vergehet, und seine Hoffnung ist eine Spinnwebe.
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
Er verlässet sich auf sein Haus und wird doch nicht bestehen; er wird sich dran halten, aber doch nicht stehen bleiben.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
Es hat wohl Früchte, ehe denn die Sonne kommt; und Reiser wachsen hervor in seinem Garten.
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
Seine Saat stehet dicke bei den Quellen und sein Haus auf Steinen.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Wenn er ihn aber verschlinget von seinem Ort, wird er sich gegen ihn stellen, als kennete er ihn nicht.
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
Siehe, das ist die Freude seines Wesens; und werden andere aus dem Staube wachsen.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
Darum siehe, daß Gott nicht verwirft die Frommen und erhält nicht die Hand der Boshaftigen,
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
bis daß dein Mund voll Lachens werde und deine Lippen voll Jauchzens.
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Die dich aber hassen; werden zuschanden werden, und der Gottlosen Hütte wird nicht bestehen.