< Yobu 8 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Mais, répondant, Baldad, le Suhite, dit:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Jusques à quand diras-tu de telles choses, et les paroles de ta bouche seront-elles comme un vent qui souffle de tout côté?
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Est-ce que Dieu pervertit le jugement, ou le Tout-Puissant subvertit-il la justice?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Quand même tes enfants auraient péché contre lui, et qu’il les aurait abandonnés à la main de leur iniquité,
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
Si toi cependant tu te lèves au point du jour pour aller vers Dieu, et que tu pries le Tout-Puissant;
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Si tu marches pur et droit, aussitôt il s’éveillera pour toi, et il donnera la paix à la demeure de ta justice;
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
Tellement que, si tes premiers biens ont été peu de chose, tes derniers seront extrêmement augmentés.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
Interroge, en effet, la génération passée, et consulte avec soin la mémoire des pères;
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
(Car nous sommes d’hier, et nous ignorons que nos jours sur la terre sont comme une ombre.)
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
Et eux-mêmes t’instruiront; ils te parleront, et c’est de leur cœur qu’ils tireront leurs paroles
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Est-ce que le jonc peut verdir sans humidité, ou le carex croître sans eau?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
Lorsqu’il est encore en fleur, et qu’il n’a pas été cueilli par une main, il sèche avant toutes les herbes.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Ainsi sont les voies de tous ceux qui oublient Dieu, et ainsi périra l’espoir de l’impie.
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
Sa folie ne lui plaira pas, et sa confiance est comme la maison de l’araignée,
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
Il s’appuiera sur sa maison, et elle ne tiendra pas debout; il l’étayera, et elle ne subsistera pas.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
Il paraît humide avant que vienne le soleil, et à son lever, son germe sortira de terre.
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
Ses racines se multiplieront sur un tas de pierres, et il s’arrêtera parmi des cailloux.
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
Si on l’arrache de sa place, elle le reniera et dira: Je ne te connais pas.
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
C’est là, en effet, la joie de sa voie, que d’autres germent ensuite de la terre.
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
Dieu ne rejette pas un homme simple, et il ne tendra pas la main à des méchants,
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
Jusqu’à ce qu’un sourire remplisse ta bouche et un cri de joie tes lèvres.
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
Ceux qui te haïssent seront couverts de confusion, et le tabernacle des impies ne subsistera pas.