< Yobu 8 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Saa tog Sjuhiten Bildad til Orde og sagde:
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
Hvor længe taler du saa, hvor længe skal Mundens Uvejr rase?
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
Mon Gud vel bøjer Retten, bøjer den Almægtige Retfærd?
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
Har dine Sønner syndet imod ham, og gav han dem deres Brøde i Vold,
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
saa søg du nu hen til Gud og bed hans Almagt om Naade!
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
Saafremt du er ren og oprigtig, ja, da vil han vaage over dig, genrejse din Retfærds Bolig;
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
din fordums Lykke vil synes ringe, saare stor skal din Fremtid blive.
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
Thi spørg dog den henfarne Slægt, læg Mærke til Fædrenes Granskning!
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
Vi er fra i Gaar, og intet ved vi, en Skygge er vore Dage paa Jord.
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
Mon ej de kan lære dig, sige dig det og give dig Svar af Hjertet:
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
Vokser der Siv, hvor der ikke er Sump, gror Nilgræs frem, hvor der ikke er Vand?
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
Endnu i Grøde, uden at høstes, visner det før alt andet Græs.
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
Saa gaar det enhver, der glemmer Gud, en vanhelligs Haab slaar fejl:
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
som Sommerspind er hans Tilflugt, hans Tillid er Spindelvæv;
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
han støtter sig til sit Hus, det falder, han klynger sig til det, ej staar det fast.
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
I Solskinnet vokser han frodigt, hans Ranker breder sig Haven over,
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
i Stendynger fletter hans Rødder sig ind, han hager sig fast mellem Sten;
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
men rives han bort fra sit Sted, fornægter det ham: »Jeg har ikke set dig!«
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
Se, det er Glæden, han har af sin Vej, og af Jorden fremspirer en anden!
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
Se, Gud agter ej den uskyldige ringe, han holder ej fast ved de ondes Haand.
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
End skal han fylde din Mund med Latter og dine Læber med Jubel;
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
dine Avindsmænd skal klædes i Skam og gudløses Telt ej findes mer!

< Yobu 8 >