< Yobu 7 >
1 “Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
¿No es el destino del hombre en la tierra una lucha? ¿No son sus días como los de un jornalero,
2 Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
Como el esclavo que anhela la sombra o como un jornalero que espera su pago?
3 choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
Así yo heredé meses sin provecho y me fueron asignadas noches de aflicción.
4 Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Cuando estoy acostado digo: ¿Cuándo me levantaré? Y la noche se alarga, y me lleno de inquietudes hasta el alba.
5 Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
Mi carne está cubierta de gusanos y de costras de polvo. Mi piel se agrieta y supura.
6 “Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Mis días se me van más veloces que la lanzadera y se me acaban sin esperanza.
7 Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Acuérdate que mi vida es un soplo. Mis ojos no volverán a ver el bien.
8 Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
El ojo del que me ve ya no me verán. Tus ojos se fijarán en mí, pero no existiré.
9 Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
Como la nube se deshace y se va, así el que baja al Seol no subirá. (Sheol )
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
No regresa a su vivienda y ya no lo reconoce su lugar.
11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
Por tanto, no refrenaré mi boca. Hablaré en la angustia de mi espíritu. Me quejaré en la amargura de mi alma.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
¿Soy yo el mar o el monstruo marino para que asignes guardia sobre mí?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
Si digo: Me consolará mi lecho, mi cama aliviará mi queja,
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
entonces me aterras con sueños y me turbas con visiones.
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
De manera que mi alma prefiere la asfixia, la muerte más bien que mis huesos.
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
Repugno la vida. No voy a vivir para siempre. Déjame, mis días son vanidad.
17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
¿Qué es el hombre para que lo engrandezcas, para que te preocupes por él,
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
para que lo examines cada mañana y lo pruebes en todo momento?
19 Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
¿Hasta cuándo no apartarás tu mirada de mí, ni me soltarás para que trague saliva?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
Si pequé, ¿cuál [daño] te hago a Ti, oh Guardián de los hombres? ¿Por qué me pones como blanco tuyo hasta convertirme en una carga para mí mismo?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”
¿Por qué no quitas mi rebelión y perdonas mi iniquidad? Porque ahora me acostaré en el polvo. Tú me buscarás, pero no estaré.