< Yobu 7 >

1 “Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
Соарта омулуй пе пэмынт есте ка а унуй осташ ши зилеле луй сунт ка але унуй мунчитор ку зиуа.
2 Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
Кум суспинэ робул дупэ умбрэ, кум ышь аштяптэ мунчиторул плата,
3 choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
аша ам еу парте де лунь де дурере, ши партя мя сунт нопць де суферинцэ.
4 Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Мэ кулк ши зик: ‘Кынд мэ вой скула? Кынд се ва сфырши ноаптя?’ Ши мэ сатур де фрэмынтэрь пынэ ын ревэрсатул зорилор.
5 Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
Трупул ми се акоперэ ку вермь ши ку о коажэ пэмынтоасэ, пеля-мь крапэ ши се десфаче.
6 “Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Зилеле меле збоарэ май юць декыт сувейка цесэторулуй, се дук ши ну май ам ничо нэдежде!
7 Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Аду-Ць аминте, Думнезеуле, кэ вяца мя есте доар о суфларе! Окий мей ну вор май ведя феричиря.
8 Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
Окюл каре мэ привеште ну мэ ва май приви; окюл Тэу мэ ва кэута ши ну вой май фи.
9 Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
Кум се рисипеште норул ши трече, аша ну се ва май ридика чел че се кобоарэ ын Локуинца морцилор! (Sheol h7585)
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
Ну се ва май ынтоарче ын каса луй ши ну-шь ва май куноаште локул ын каре локуя.
11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
Де ачея ну-мь вой цине гура, чи вой ворби ын нелиништя инимий меле, мэ вой тынгуи ын амэрэчуня суфлетулуй меу.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
Оаре о маре сунт еу сау ун балаур де маре, де-ай пус стражэ ын журул меу?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
Кынд зик: ‘Патул мэ ва ушура, кулкушул ымь ва алина дурериле’,
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
атунч мэ ынспэймынць прин висе, мэ ынгрозешть прин ведений.
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
Ах, аш вря май бине гытуиря, май бине моартя декыт ачесте оасе!
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
Ле диспрецуеск!… Ну вой трэи ын вечь… Ласэ-мэ, кэч доар о суфларе ми-й вяца!
17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
Че есте омул ка сэ-Ць песе атыт де мулт де ел, ка сэ ей сяма ла ел,
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
сэ-л черчетезь ын тоате диминециле ши сэ-л ынчерчь ын тоате клипеле?
19 Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
Кынд вей ынчета одатэ сэ мэ привешть? Кынд ымь вей да рэгаз сэ-мь ынгит скуйпатул?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
Дакэ ам пэкэтуит, че пот сэ-Ць фак, Пэзиторул оаменилор? Пентру че м-ай пус цинтэ сэӂецилор Тале, де ам ажунс о поварэ кяр пентру мине ынсумь?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”
Пентру че ну-мь ерць пэкатул ши пентру че ну-мь уйць фэрэделеӂя? Кэч вой адорми ын цэрынэ ши, кынд мэ вей кэута, ну вой май фи!”

< Yobu 7 >