< Yobu 7 >
1 “Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
Vai cilvēkam nav karš virs zemes, un vai viņa dienas nav kā algādža dienas?
2 Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
Tā kā kalps ilgojās pēc ēnas un kā algādzis gaida uz savu algu,
3 choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
Tāpat man nākuši daudz bēdīgi mēneši, un grūtas naktis man ir piešķirtas.
4 Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Kad apguļos, tad es saku: kad atkal celšos? un vakars vilcinājās, un es apnīkstu mētāties gultā līdz gaismai.
5 Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
Mana miesa ir apsegta ar tārpiem un vātīm, mana āda sadzīst un čūlo atkal.
6 “Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Manas dienas ir ātrākas nekā vēvera (audēja) spole un beidzās bez nekādas cerības.
7 Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Piemini, ka mana dzīvība ir vējš un mana acs labuma vairs neredzēs.
8 Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
Acs, kas nu mani redz, manis vairs neredzēs. Tavas acis uz mani skatās, un es vairs neesmu.
9 Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
Mākonis iznīkst un aiziet, - tāpat kas kapā nogrimst, nenāks atkal augšām. (Sheol )
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
Viņš neatgriezīsies atkal savā namā, un viņa vieta viņu vairs nepazīs.
11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
Tā tad es savu muti neturēšu, es runāšu savās sirds bēdās, es žēlošos savā sirdsrūgtumā.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
Vai tad es esmu kā jūra, vai kā liela jūras zivs, ka tu ap mani noliec vakti?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
Kad es saku: mana gulta man iepriecinās, manas cisas atvieglinās manas vaimanas,
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
Tad Tu mani izbiedē ar sapņiem, un caur parādīšanām Tu mani iztrūcini,
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
Tā ka mana dvēsele vēlās būt nožņaugta, labāki mirt nekā tā izģinst.
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
Es esmu apnicis, man netīk mūžam dzīvot; atstājies jel no manis, jo manas dienas ir kā nekas.
17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
Kas ir cilvēks, ka Tu viņu tik augsti turi un ka Tu viņu lieci vērā,
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
Un viņu piemeklē ik rītu, viņu pārbaudi ik acumirkli,
19 Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
Ka Tu nemaz no manis neatstājies un mani nepameti, ne siekalas ierīt?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
Ja esmu grēkojis, ko es Tev darīšu, Tu cilvēku sargs? Kāpēc Tu mani esi licis Sev par mērķi, ka es sev pašam palicis par nastu?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”
Un kāpēc Tu manus pārkāpumus nepiedod un neatņem manu noziegumu? Jo nu es apgulšos pīšļos, un kad Tu mani meklēsi, tad manis vairs nebūs.