< Yobu 5 >
1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
AHORA pues da voces, si habrá quien te responda; ¿y á cuál de los santos te volverás?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Es cierto que al necio la ira lo mata, y al codicioso consume la envidia.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Yo he visto al necio que echaba raíces, y en la misma hora maldije su habitación.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Sus hijos estarán lejos de la salud, y en la puerta serán quebrantados, y no habrá quien los libre.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Su mies comerán los hambrientos, y sacaránla de entre las espinas, y los sedientos beberán su hacienda.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Porque la iniquidad no sale del polvo, ni la molestia brota de la tierra.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
Empero como las centellas se levantan para volar por [el aire], así el hombre nace para la aflicción.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Ciertamente yo buscaría á Dios, y depositaría en él mis negocios:
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
El cual hace cosas grandes é inescrutables, y maravillas que no tienen cuento:
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Que da la lluvia sobre la haz de la tierra, y envía las aguas por los campos:
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Que pone los humildes en altura, y los enlutados son levantados á salud:
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Que frustra los pensamientos de los astutos, para que sus manos no hagan nada:
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Que prende á los sabios en la astucia de ellos, y el consejo de los perversos es entontecido;
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
De día se topan con tinieblas, y en mitad del día andan á tientas como de noche:
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Y libra de la espada al pobre, de la boca de los impíos, y de la mano violenta;
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
Pues es esperanza al menesteroso, y la iniquidad cerrará su boca.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
He aquí, bienaventurado es el hombre á quien Dios castiga: por tanto no menosprecies la corrección del Todopoderoso.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
Porque él es el que hace la llaga, y él [la] vendará: él hiere, y sus manos curan.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
En seis tribulaciones te librará, y en la séptima no te tocará el mal.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
En el hambre te redimirá de la muerte, y en la guerra de las manos de la espada.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Del azote de la lengua serás encubierto; ni temerás de la destrucción cuando viniere.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
De la destrucción y del hambre te reirás, y no temerás de las bestias del campo:
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
Pues aun con las piedras del campo tendrás tu concierto, y las bestias del campo te serán pacíficas.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
Y sabrás que hay paz en tu tienda; y visitarás tu morada, y no pecarás.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Asimismo echarás de ver que tu simiente es mucha, y tu prole como la hierba de la tierra.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Y vendrás en la vejez á la sepultura, como el montón de trigo que se coge á su tiempo.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
He aquí lo que hemos inquirido, lo cual es así: óyelo, y juzga tú para contigo.