< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Стригэ акум! Чине ыць ва рэспунде? Кэруя динтре сфинць ый вей ворби?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Небунул пере учис де мыния луй, простул моаре учис де априндеря луй.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Ам вэзут пе ун небун принзынд рэдэчинэ; апой, деодатэ, й-ам блестемат локуинца.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Фиий луй н-ау норок, сунт кэлкаць ын пичоаре ла поартэ, ши нимень ну-й скапэ!
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Сечеришул луй есте мынкат де чей флэмынзь, каре вин сэ-л я кяр ши дин спинь, ши авериле луй сунт ынгиците де оамень ынсетаць.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Ненорочиря ну рэсаре дин цэрынэ, ши суферинца ну ынколцеште дин пэмынт.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
Омул се наште ка сэ суфере, дупэ кум скынтея се наште ка сэ збоаре.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Еу аш алерга ла Думнезеу, луй Думнезеу Й-аш спуне неказул меу.
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
Ел фаче лукрурь марь ши непэтрунсе, минунь фэрэ нумэр.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Ел варсэ плоая пе пэмынт ши тримите апэ пе кымпий.
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Ел ыналцэ пе чей смериць ши избэвеште пе чей некэжиць.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Ел нимичеште плануриле оаменилор виклень, ши мыниле лор ну пот сэ ле ымплиняскэ.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Ел принде пе чей ынцелепць ын викления лор, ши плануриле оаменилор ыншелэторь сунт рэстурнате:
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
дау песте ынтунерик ын мижлокул зилей, быжбые зиуа-н амяза маре ка ноаптя.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Астфел, Думнезеу окротеште пе чел слаб ымпотрива аменинцэрилор лор ши-л скапэ дин мына челор путерничь,
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
аша ынкыт нэдеждя сприжинэ пе чел ненорочит, яр фэрэделеӂя ышь ынкиде гура.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Фериче де омул пе каре-л чартэ Думнезеу! Ну несокоти мустраря Челуй Атотпутерник.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
Ел фаче рана ши тот Ел о лягэ; Ел рэнеште, ши мына Луй тэмэдуеште.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
Де шасе орь те ва избэви дин неказ ши де шапте орь ну те ва атинӂе рэул.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
Ел те ва скэпа де моарте ын време де фоамете ши де ловитуриле сабией ын време де рэзбой.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Вей фи ла адэпост де бичул лимбий, вей фи фэрэ тямэ кынд ва вени пустииря.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
Вей рыде де пустиире, ка ши де фоамете, ши ну вей авя сэ те темь де фяреле пэмынтулуй.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
Кэч вей фаче легэмынт пынэ ши ку петреле кымпулуй, ши фяреле пэмынтулуй вор фи ын паче ку тине.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
Вей авя феричире ын кортул тэу, ыць вей гэси турмеле ынтреӂь,
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
ыць вей ведя сэмынца крескынду-ць ши одраслеле ынмулцинду-се ка ярба де пе кымп.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Вей интра ын мормынт ла бэтрынеце, ка снопул стрынс ла время луй.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Ятэ че ам черчетат, ши аша есте! Аскултэ, кэ сунт спре фолосул тэу!”

< Yobu 5 >