< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
«الان استغاثه کن و آیا کسی هست که تو راجواب دهد؟ و به کدامیک از مقدسان توجه خواهی نمود؟۱
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
زیرا غصه، احمق رامی کشد و حسد، ابله را می‌میراند.۲
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
من احمق رادیدم که ریشه می‌گرفت و ناگهان مسکن او رانفرین کردم.۳
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
فرزندان او از امنیت دور هستند ودر دروازه پایمال می‌شوند و رهاننده‌ای نیست.۴
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
که گرسنگان محصول او را می‌خورند، و آن رانیز از میان خارها می‌چینند، و دهان تله برای دولت ایشان باز است.۵
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
زیرا که بلا از غبار درنمی آید، و مشقت از زمین نمی روید.۶
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
بلکه انسان برای مشقت مولود می‌شود، چنانکه شراره‌ها بالامی پرد.۷
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
و لکن من نزد خدا طلب می‌کردم، ودعوی خود را بر خدا می‌سپردم،۸
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
که اعمال عظیم و بی‌قیاس می‌کند و عجایب بی‌شمار؛۹
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
که بر روی زمین باران می‌باراند، و آب بر روی صخره‌ها جاری می‌سازد،۱۰
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
تا مسکینان را به مقام بلند برساند، و ماتمیان به سلامتی سرافراشته شوند.۱۱
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
که فکرهای حیله گران را باطل می‌سازد، به طوری که دستهای ایشان هیچ کار مفیدنمی تواند کرد.۱۲
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
که حکیمان را در حیله ایشان گرفتار می‌سازد، و مشورت مکاران مشوش می‌شود.۱۳
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
در روز به تاریکی برمی خورند و به وقت ظهر، مثل شب کورانه راه می‌روند.۱۴
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
که مسکین را از شمشیر دهان ایشان، و از دست زورآور نجات می‌دهد.۱۵
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
پس امید، برای ذلیل پیدا می‌شود و شرارت دهان خود را می‌بندد.۱۶
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
«هان، خوشابحال شخصی که خدا تنبیهش می‌کند. پس تادیب قادر مطلق را خوار مشمار.۱۷
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
زیرا که او مجروح می‌سازد و التیام می‌دهد، ومی کوبد و دست او شفا می‌دهد.۱۸
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
در شش بلا، تو را نجات خواهد داد و در هفت بلا، هیچ ضرر برتو نخواهد رسید.۱۹
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
در قحط تو را از موت فدیه خواهد داد، و در جنگ از دم شمشیر.۲۰
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
ازتازیانه زبان پنهان خواهی ماند، و چون هلاکت آید، از آن نخواهی ترسید.۲۱
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
بر خرابی وتنگسالی خواهی خندید، و از وحوش زمین بیم نخواهی داشت.۲۲
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
زیرا با سنگهای صحراهمداستان خواهی بود، و وحوش صحرا با توصلح خواهند کرد.۲۳
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
و خواهی دانست که خیمه تو ایمن است، و مسکن خود را تجسس خواهی کرد و چیزی مفقود نخواهی یافت.۲۴
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
وخواهی دانست که ذریتت کثیر است و اولاد تومثل علف زمین.۲۵
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
و در شیخوخیت به قبرخواهی رفت، مثل بافه گندم که در موسمش برداشته می‌شود.۲۶
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
اینک این را تفتیش نمودیم وچنین است، پس تو این را بشنو و برای خویشتن بدان.»۲۷

< Yobu 5 >