< Yobu 5 >
1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Rop du bare! Er det vel nogen som svarer dig? Og til hvem av de hellige vil du vende dig?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
For harme slår dåren ihjel, og vrede dreper den tåpelige.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Jeg så en dåre skyte røtter; men med ett måtte jeg rope ve over hans bolig.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Hans barn var uten hjelp; de blev trådt ned i porten, og det var ingen som frelste dem.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
De hungrige åt op hans avling, ja, midt ut av torner hentet de den, og snaren lurte på hans gods.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
For ikke skyter ulykke op av støvet, og møie spirer ikke frem av jorden;
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
men mennesket fødes til møie, likesom ildens gnister flyver høit i været.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Men jeg vilde vende mig til Gud og overlate min sak til ham,
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
han som gjør store, uransakelige ting, under uten tall,
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
som sender regn utover jorden og lar vann strømme utover markene,
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
som ophøier de ringe og lar de sørgende nå frem til frelse,
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
som gjør de kløktiges råd til intet, så deres hender ikke får utrettet noget som varer,
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
han som fanger de vise i deres kløkt og lar de listiges råd bli forhastet;
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
om dagen støter de på mørke, og om middagen famler de som om natten.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Og således frelser han den fattige fra sverdet, fra deres munn og fra den sterkes hånd,
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
og det blir håp for den ringe, og ondskapen må lukke sin munn.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Ja, salig er det menneske Gud refser, og den Allmektiges tukt må du ikke akte ringe!
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
For han sårer, og han forbinder; han slår, og hans hender læger.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
I seks trengsler skal han berge dig, og i den syvende skal intet ondt røre dig.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
I hungersnød frir han dig fra døden og i krig fra sverdets vold.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
For tungens svepe skal du være skjult, og du skal ikke frykte når ødeleggelsen kommer.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
Ødeleggelse og hunger skal du le av, og for jordens ville dyr skal du ikke frykte;
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
for med markens stener står du i pakt, og markens ville dyr holder fred med dig.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
Og du skal få se at ditt telt er trygt, og ser du over din eiendom, skal du intet savne.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Og du skal få se at din ætt blir tallrik, og dine efterkommere som jordens urter.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Du skal i fullmoden alder gå i graven, likesom kornbånd føres inn sin tid.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Se, dette er det vi har utgransket, og således er det. Hør det og merk dig det!