< Yobu 5 >
1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Ake umemeze, ukhona ongakuphendula yini? Uzaphendukela kuwuphi wabangcwele?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Ngoba ulaka luyasibulala isiwula, lomhawu ubulale isiphukuphuku.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Mina ngibone isiwula sigxila, kodwa ngahle ngaqalekisa indawo yaso yokuhlala.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Abantwana baso bakhatshana losindiso, bachothozwa esangweni, njalo kungekho umkhululi.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Osivuno saso olambileyo uyasidla, esithatha lemeveni, lomphangi uginya inotho yaso.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Ngoba usizi kaluveli ethulini, lenhlupheko kayihlumi emhlabathini.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
Kube kanti umuntu uzalelwe inhlupheko njengoba inhlansi ziqhatshela phezulu.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Kodwa mina bengizadinga uNkulunkulu, lakuNkulunkulu bengizabeka udaba lwami.
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
Owenza izinto ezinkulu lezingelakuhlolwa, imimangaliso engelakubalwa.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Onika izulu ebusweni bomhlaba, athumele amanzi ebusweni bamaphandle,
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
ukuze abamise phezulu abaphansi, ukuze abalilayo baphakanyiselwe ekuvikelekeni.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Uchitha amacebo abalobuqili, ukuze izandla zabo zingenzi cebo.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Ubamba abahlakaniphileyo ebuqilini babo, ukuze icebo labangaqondanga liwiselwe phansi.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
Bahlangana lomnyama emini, baphumputhe phakathi kwemini njengebusuku.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Kodwa ukhulula umyanga enkembeni, emlonyeni wabo, lesandleni solamandla.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
Ngakho umyanga ulethemba, lobubi buzavala umlomo wabo.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Khangela, ubusisiwe lowomuntu uNkulunkulu amlayayo; ngakho ungadeleli ukukhuza kukaSomandla.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
Ngoba yena uzwisa ubuhlungu, abuye abophe; uyalimaza, lezandla zakhe ziyapholisa.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
Uzakukhulula enhluphekweni eziyisithupha, lakweziyisikhombisa ububi kabuyikukuthinta.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
Endlaleni uzakuhlenga ekufeni, lempini emandleni enkemba.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Uzafihlelwa isiswepu solimi, njalo kawuyikwesaba incithakalo lapho ifika.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
Uzahleka incithakalo lendlala, njalo kawuyikwesaba izilo zomhlaba.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
Ngoba uzakuba lesivumelwano lamatshe eganga, lezilo zeganga zizakuba lokuthula lawe.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
Njalo uzakwazi ukuthi ithente lakho lilokuthula, uzakwethekela indawo yakho yokuhlala ungasweli lutho.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Uzakwazi futhi ukuthi inzalo yakho izakuba nengi, lembewu yakho njengotshani bomhlaba.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Uzafika engcwabeni lakho usuluphele, njengenqumbi zamabele zisenyuka ngesikhathi sawo.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Khangela lokhu, sesikuhlolile; kunjalo. Kuzwe, uzazele wena.