< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Voca ergo, si est qui tibi respondeat, et ad aliquem sanctorum convertere.
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Vere stultum interficit iracundia, et parvulum occidit invidia.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Ego vidi stultum firma radice, et maledixi pulchritudini eius statim.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Longe fient filii eius a salute, et conterentur in porta, et non erit qui eruat.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Cuius messem famelicus comedet, et ipsum rapiet armatus, et bibent sitientes divitias eius.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Nihil in terra sine causa fit, et de humo non oritur dolor.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
Homo nascitur ad laborem, et avis ad volatum.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Quam ob rem ego deprecabor Dominum, et ad Deum ponam eloquium meum:
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
Qui facit magna et inscrutabilia et mirabilia absque numero:
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Qui dat pluviam super faciem terrae, et irrigat aquis universa:
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Qui ponit humiles in sublime, et moerentes erigit sospitate:
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Qui dissipat cogitationes malignorum, ne possint implere manus eorum quod coeperant:
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Qui apprehendit sapientes in astutia eorum, et consilium pravorum dissipat:
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
Per diem incurrent tenebras, et quasi in nocte sic palpabunt in meridie.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Porro salvum faciet egenum a gladio oris eorum, et de manu violenti pauperem.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
Et erit egeno spes, iniquitas autem contrahet os suum.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Beatus homo qui corripitur a Deo: increpationem ergo Domini ne reprobes:
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
Quia ipse vulnerat, et medetur: percutit, et manus eius sanabunt.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
In sex tribulationibus liberabit te, et in septima non tangent te malum.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
In fame eruet te de morte, et in bello de manu gladii.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
A flagello linguae absconderis, et non timebis calamitatem cum venerit.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
In vastitate, et fame ridebis, et bestias terrae non formidabis.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
Sed cum lapidibus regionum pactum tuum, et bestiae terrae pacificae erunt tibi.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
Et scies quod pacem habeat tabernaculum tuum, et visitans speciem tuam, non peccabis.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Scies quoque quoniam multiplex erit semen tuum, et progenies tua quasi herba terrae.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Ingredieris in abundantia sepulchrum, sicut infertur acervus tritici in tempore suo.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Ecce, hoc, ut investigavimus, ita est: quod auditum, mente pertracta.

< Yobu 5 >