< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
« Appelle maintenant; y a-t-il quelqu'un qui te réponde? Vers lequel des saints vous tournerez-vous?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Car la rancune tue l'homme insensé, et la jalousie tue les simples.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
J'ai vu l'insensé prendre racine, mais j'ai soudainement maudit son habitation.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Ses enfants sont loin de la sécurité. Ils sont écrasés dans la porte. Il n'y en a pas non plus pour les délivrer,
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
dont la récolte est dévorée par les affamés, et le sortir même des épines. Le piège s'ouvre pour leur substance.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Car l'affliction ne sort pas de la poussière, Les problèmes ne sortent pas non plus du sol;
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
mais l'homme est né pour les problèmes, alors que les étincelles volent vers le haut.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
« Quant à moi, je chercherais Dieu. Je confierais ma cause à Dieu,
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
qui fait de grandes choses qui ne peuvent pas être sondées, des choses merveilleuses sans nombre;
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
qui donne la pluie sur la terre, et envoie des eaux sur les champs;
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
afin qu'il élève en haut ceux qui sont bas, ceux qui pleurent sont élevés en sécurité.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Il fait échouer les plans des rusés, de sorte que leurs mains ne peuvent pas accomplir leur entreprise.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Il prend les sages dans leur propre ruse; le conseil des rusés est porté à bout de bras.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
Ils rencontrent les ténèbres pendant le jour, et tâtonnent à midi comme dans la nuit.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Mais il sauve de l'épée de leur bouche, même le nécessiteux de la main des puissants.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
Le pauvre a donc de l'espoir, et l'injustice lui fait fermer la bouche.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
« Voici, heureux l'homme que Dieu corrige. Ne méprisez donc pas le châtiment du Tout-Puissant.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
Car il blesse et panse. Il blesse et ses mains réparent.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
Il te délivrera dans six épreuves; Oui, en sept, aucun mal ne vous touchera.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
Dans la famine, il te rachètera de la mort; dans la guerre, de la puissance de l'épée.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Tu seras à l'abri du fléau de la langue, vous n'aurez pas non plus peur de la destruction quand elle viendra.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
Vous rirez de la destruction et de la famine, vous n'aurez pas non plus peur des animaux de la terre.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
Car vous serez alliés aux pierres des champs. Les animaux des champs seront en paix avec vous.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
Tu sauras que ta tente est en paix. Vous visiterez votre pli, et ne manquerez rien.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Tu sauras aussi que ta descendance sera grande, ta progéniture comme l'herbe de la terre.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Tu viendras au tombeau dans un âge avancé, comme un choc de grain vient en sa saison.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Voici, nous avons fait des recherches. Il en est ainsi. Entendez-le, et sachez que c'est pour votre bien. »

< Yobu 5 >