< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
"Call now; is there any who will answer you? To which of the holy ones will you turn?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
For resentment kills the foolish man, and jealousy kills the simple.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
I have seen the foolish taking root, but suddenly I cursed his habitation.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
His children are far from safety. They are crushed in the gate. Neither is there any to deliver them,
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
whose harvest the hungry eats up, and take it even out of the thorns. And the thirsty swallow up their wealth.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
For affliction doesn't come forth from the dust, neither does trouble spring out of the ground;
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
but man is born to trouble, as the sparks fly upward.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
"But as for me, I would seek God. I would commit my cause to God,
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
who does great things that can't be fathomed, marvelous things without number;
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
who gives rain on the earth, and sends waters on the fields;
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
so that he sets up on high those who are low, those who mourn are exalted to safety.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
He frustrates the devices of the crafty, So that their hands can't perform their enterprise.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
He traps the wise in their own craftiness, and the counsel of the cunning are brought to a quick end.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
They meet with darkness in the day time, and grope at noonday as in the night.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
But he saves from the sword of their mouth, even the needy from the hand of the mighty.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
So the poor has hope, and injustice shuts her mouth.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
"Look, blessed is the man whom God corrects. Therefore do not despise the chastening of Shaddai.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
For he wounds, and binds up. He injures, and his hands make whole.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
He will deliver you in six troubles; yes, in seven there shall no evil touch you.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
In famine he will redeem you from death; in war, from the power of the sword.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
You shall be hidden from the scourge of the tongue, neither shall you be afraid of destruction when it comes.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
At destruction and famine you shall laugh, neither shall you be afraid of the animals of the earth.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
For you shall be in league with the stones of the field. The animals of the field shall be at peace with you.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
You shall know that your tent is in peace. You shall visit your fold, and shall miss nothing.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
You shall know also that your descendants shall be great, and your offspring as the grass of the earth.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
You shall come to your grave in a full age, like a shock of grain comes in its season.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Look this, we have searched it, so it is. Hear it, and know it for your good."

< Yobu 5 >