< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Call now if there be any that will answer thee, and turn to some of the saints.
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Anger indeed killeth the foolish, and envy slayeth the little one.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
I have seen a fool with a strong root, and I cursed his beauty immediately.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
His children shall be far from safety, and shall be destroyed in the gate, and there shall be none to deliver them.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Whose harvest the hungry shall eat, and the armed man shall take him by violence, and the thirsty shall drink up his riches.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Nothing upon earth is done without a voice cause, and sorrow doth not spring out of the ground.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
Man is born to labour and the bird to fly.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Wherefore I will pray to the Lord, and address my speech to God:
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
Who doth great things and unsearchable and wonderful things without number:
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Who giveth rain upon the face of the earth, and watereth all things with waters:
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Who setteth up the humble on high, and comforteth with health those that mourn.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Who bringeth to nought the designs of the malignant, so that their hands cannot accomplish what they had begun:
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Who catcheth the wise in their craftiness, and disappointeth the counsel of the wicked:
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
They shall meet with darkness in the day, and grope at noonday as in the night.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
But he shall save the needy from the sword of their mouth, and the poor from the hand of the violent.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
And to the needy there shall he hope, but iniquity shall draw in her mouth.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Blessed is the mall whom God correcteth: refuse not therefore the chastising of the lord:
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
For he woundeth, and cureth: he striketh, and his hands shall heal.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
In six troubles he shall deliver thee, and in the seventh, evil shall not touch thee.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
In famine he shall deliver thee from death: and in battle, from the hand of the sword.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Thou shalt he hidden from the scourge of the tongue: and thou shalt not fear calamity when it cometh.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
In destruction and famine then shalt laugh: and thou shalt not be afraid of the beasts of the earth.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
But thou shalt have a covenant with the stones of the lands, and the beasts of the earth shall be at pence with thee.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
And thou shalt know that thy tabernacle is in peace, and visiting thy beauty thou shalt not sin.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Thou shalt know also that thy seed shall be multiplied, and thy offspring like the grass of the earth.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Thou shalt enter into the grave in abundance, as a heap of wheat is brought in its season.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Behold, this is even so, as we have searched out: which thou having heard, consider it thoroughly in thy mind.

< Yobu 5 >