< Yobu 5 >
1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Call, I pray thee! Is there any that answereth thee? and to which of the holy ones wilt thou turn?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
For vexation killeth the foolish man, and envy slayeth the simple.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
I myself saw the foolish taking root, but suddenly I cursed his habitation.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
His children are far from safety, and they are crushed in the gate, and there is no deliverer:
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Whose harvest the hungry eateth up, and taketh even out of the thorns; and the snare gapeth for his substance.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
For evil cometh not forth from the dust, neither doth trouble spring out of the ground;
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
For man is born to trouble, as the sparks fly upwards.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
But as for me I will seek unto God, and unto God commit my cause;
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
Who doeth great things and unsearchable, marvellous things without number;
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Who giveth rain on the face of the earth, and sendeth waters on the face of the fields;
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Setting up on high those that are low; and mourners are exalted to prosperity.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
He disappointeth the devices of the crafty, and their hands carry not out the enterprise.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
He taketh the wise in their own craftiness; and the counsel of the wily is carried headlong:
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
They meet with darkness in the daytime, and grope at midday as in the night.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
And he saveth the needy from the sword, from their mouth, and from the hand of the mighty.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
So the poor hath what he hopeth for, and unrighteousness stoppeth her mouth.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Behold, happy is the man whom God correcteth; therefore despise not the chastening of the Almighty.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
For he maketh sore, and bindeth up; he woundeth, and his hands make whole.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
He will deliver thee in six troubles, and in seven there shall no evil touch thee.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
In famine he will redeem thee from death, and in war from the power of the sword.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Thou shalt be hidden from the scourge of the tongue; and thou shalt not be afraid of destruction when it cometh.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
At destruction and famine thou shalt laugh, and of the beasts of the earth thou shalt not be afraid.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
For thou shalt be in league with the stones of the field, and the beasts of the field shall be at peace with thee.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
And thou shalt know that thy tent is in peace; and thou wilt survey thy fold, and miss nothing.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
And thou shalt know that thy seed is numerous, and thine offspring as the herb of the earth.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Thou shalt come to the grave in a ripe age, as a shock of corn is brought in in its season.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Behold this, we have searched it out, so it is; hear it, and know thou it for thyself.