< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Call now, is there any who will answer thee? And to which of the holy ones will thou turn?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
For vexation kills the foolish man, and jealousy slays the silly one.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
I have seen the foolish taking root, but suddenly I cursed his habitation.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
His sons are far from safety, and they are crushed in the gate. Neither is there any to deliver them,
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
whose harvest the hungry eat up, and takes it even out of the thorns, and the snare gapes for their substance.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
For affliction does not come forth from the dust, nor does trouble spring out of the ground,
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
but man is born to trouble, as the sparks fly upward.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
But as for me, I would seek to God. And to God I would commit my cause,
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
who does great things and unsearchable, marvelous things without number,
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
who gives rain upon the earth, and sends waters upon the fields,
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
so that he sets up on high those who are low, and those who mourn are exalted to safety.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
He frustrates the devices of the crafty so that their hands cannot perform their enterprise.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
He takes the wise in their own craftiness, and the counsel of the cunning is carried headlong.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
They meet with darkness in the daytime, and grope at noonday as in the night.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
But he saves from the sword of their mouth, even the needy from the hand of the mighty.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
So a poor man has hope, and iniquity stops her mouth.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Behold, happy is the man whom God corrects. Therefore do not despise thou the chastening of the Almighty.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
For he injures, and binds up. He wounds, and his hands make whole.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
He will deliver thee in six troubles. Yea, in seven there shall no evil touch thee.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
In famine he will redeem thee from death, and in war from the power of the sword.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Thou shall be hid from the scourge of the tongue. Neither shall thou be afraid of destruction when it comes.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
At destruction and dearth thou shall laugh, nor shall thou be afraid of the beasts of the earth.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
For thou shall be in league with the stones of the field, and the beasts of the field shall be at peace with thee.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
And thou shall know that thy tent is in peace, and thou shall visit thy fold, and shall miss nothing.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
Thou shall know also that thy seed shall be great, and thine offspring as the grass of the earth.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Thou shall come to thy grave in a full age, like a shock of grain comes in its season.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Lo this, we have searched it, so it is. Hear it, and know thou it for thy good.

< Yobu 5 >