< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Råb kun! Giver nogen dig Svar? Og til hvem af de Hellige vender du dig?
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Thi Dårens Harme koster ham Livet, Tåbens Vrede bliver hans Død.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Selv har jeg set en Dåre rykkes op, hans Bolig rådne brat;
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
hans Sønner var uden Hjælp, trådtes ned i Porten, ingen reddede dem;
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
sultne åd deres Høst, de tog den, selv mellem Torne, og tørstige drak deres Mælk.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Thi Vanheld vokser ej op af Støvet, Kvide spirer ej frem af Jorden,
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
men Mennesket avler Kvide, og Gnisterne flyver til Vejrs.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Nej, jeg vilde søge til Gud og lægge min Sag for ham,
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
som øver ufattelig Vælde og Undere uden Tal,
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
som giver Regn på Jorden og nedsender Vand over Marken
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
for at løfte de bøjede højt, så de sørgende opnår Frelse,
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
han, som krydser de kloges Tanker, så de ikke virker noget, der varer,
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
som fanger de vise i deres Kløgt, så de listiges Råd er forhastet;
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
i Mørke raver de, selv om Dagen, famler ved Middag, som var det Nat.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Men han frelser den arme fra Sværdet og fattig af stærkes Hånd,
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
så der bliver Håb for den ringe og Ondskaben lukker sin Mund.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Held den Mand, som revses at Gud; ringeagt ej den Almægtiges Tugt!
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
Thi han sårer, og han forbinder, han slår, og hans Hænder læger.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
Seks Gange redder han dig i Trængsel, syv går Ulykken uden om dig;
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
han frier dig fra Døden i Hungersnød, i Krig fra Sværdets Vold;
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
du er gemt for Tungens Svøbe, har intet at frygte, når Voldsdåd kommer;
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
du ler ad Voldsdåd og Hungersnød og frygter ej Jordens vilde dyr;
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
du har Pagt med Markens Sten, har Fred med Markens Vilddyr;
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
du kender at have dit Telt i Fred, du mønstrer din Bolig, og intet fattes;
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
du kender at have et talrigt Afkom, som Jordens Urter er dine Spirer;
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
Graven når du i Ungdomskraft, som Neg føres op, når Tid er inde.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Se, det har vi gransket, således er det; det har vi hørt, så vid også du det!

< Yobu 5 >