< Yobu 42 >

1 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
Da svarte Job Herren og sa:
2 “Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
Jeg vet at du kan alt, og at ingen tanke er umulig å utføre for dig.
3 Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
Hvem er den som vil formørke ditt råd i uforstand? Derfor må jeg si: Jeg har talt om det jeg ikke forstod, om det som var mig for underlig, og som jeg ikke skjønte.
4 “Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
Men hør nu, så vil jeg tale! Jeg vil spørre dig, og du skal lære mig.
5 Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
Bare hvad ryktet meldte, hadde jeg hørt om dig; men nu har mitt øie sett dig.
6 Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
Derfor kaller jeg alt tilbake og angrer i støv og aske.
7 Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
Da Herren hadde talt disse ord til Job, sa han til Elifas fra Teman: Min vrede er optendt mot dig og dine to venner; for I har ikke talt rett om mig, som min tjener Job.
8 Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
Ta derfor syv okser og syv værer og gå til min tjener Job og ofre dem som brennoffer for eder! Og min tjener Job skal bede for eder; bare ham vil jeg bønnhøre, så jeg ikke gjør med eder efter eders uforstand; for I har ikke talt rett om mig, som min tjener Job.
9 Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
Så gikk Elifas fra Teman og Bildad fra Suah og Sofar fra Na'ama og gjorde som Herren hadde talt til dem; og Herren bønnhørte Job.
10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
Og Herren gjorde ende på Jobs ulykke, da han bad for sine venner; og Herren øket alt det Job hadde hatt, til det dobbelte.
11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
Og alle hans brødre kom til ham, og alle hans søstre og alle som hadde kjent ham før, og de åt med ham i hans hus og viste ham medynk og trøstet ham for all den ulykke Herren hadde latt komme over ham; og de gav ham hver en kesitte og hver en gullring.
12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
Og Herren velsignet Jobs siste dager mere enn hans første, og han fikk fjorten tusen får og seks tusen kameler og tusen par okser og tusen aseninner.
13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
Og han fikk syv sønner og tre døtre.
14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
Den ene datter kalte han Jemima, den annen Kesia og den tredje Keren-Happuk.
15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
Så fagre kvinner som Jobs døtre fantes ikke i hele landet; og deres far gav dem arv blandt deres brødre.
16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
Derefter levde Job hundre og firti år, og han så sine barn og barnebarn i fjerde ledd.
17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.
Og Job døde, gammel og mett av dager.

< Yobu 42 >